< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
Думнезеуле, ам аузит ку урекиле ноастре ши пэринций ноштри не-ау повестит лукрэриле пе каре ле-ай фэкут пе время лор, ын зилеле де одиниоарэ.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Ку мына Та ай изгонит нямурь ка сэ-й сэдешть пе ей, ай ловит попоаре ка сэ-й ынтинзь пе ей.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
Кэч ну прин сабия лор ау пус мына пе царэ, ну брацул лор й-а мынтуит, чи дряпта Та, брацул Тэу, лумина Фецей Тале, пентру кэ ый юбяй.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
Думнезеуле, Ту ешть Ымпэратул меу: порунчеште избэвиря луй Иаков!
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Ку Тине доборым пе врэжмаший ноштри, ку Нумеле Тэу здробим пе потривничий ноштри.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
Кэч ну ын аркул меу мэ ынкред, ну сабия мя мэ ва скэпа;
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
чи Ту не избэвешть де врэжмаший ноштри ши дай де рушине пе чей че не урэск.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
Ной, ын фиекаре зи, не лэудэм ку Думнезеу ши пуруря слэвим Нумеле Тэу.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
Дар Ту не лепезь, не акоперь де рушине, ну май ешь ку оштириле ноастре;
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
не фачь сэ дэм досул ынаинтя врэжмашулуй, ши чей че не урэск ридикэ прэзь луате де ла ной.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Не дай ка пе ниште ой де мынкат ши не рисипешть принтре нямурь.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Винзь пе попорул Тэу пе нимик ши ну-л сокотешть де маре прец.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Не фачь де окара вечинилор ноштри, де батжокура ши де рысул челор че не ынконжоарэ.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Не фачь де поминэ принтре нямурь ши причинэ де клэтинаре дин кап принтре попоаре.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
Окара мя есте тотдяуна ынаинтя мя ши рушиня ымь акоперэ фаца
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
ла гласул челуй че мэ батжокореште ши мэ окэрэште, ла ведеря врэжмашулуй ши рэзбунэторулуй.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
Тоате ачестя ни се ынтымплэ фэрэ ка ной сэ Те фи уйтат, фэрэ сэ фи кэлкат легэмынтул Тэу:
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
да, инима ну ни с-а абэтут, паший ну ни с-ау депэртат де пе кэраря Та,
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
ка сэ не здробешть ын локуинца шакалилор ши сэ не акоперь ку умбра морций.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Дакэ ам фи уйтат Нумеле Думнезеулуй ностру ши не-ам фи ынтинс мыниле спре ун думнезеу стрэин,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
н-ар шти Думнезеу лукрул ачеста, Ел, каре куноаште тайнеле инимий?
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Дар дин причина Та сунтем ынжунгияць ын тоате зилеле, сунтем привиць ка ниште ой сортите пентру мэчелэрие.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Трезеште-Те! Пентру че дормь, Доамне? Трезеште-Те! Ну не лепэда пе вечие!
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Пентру че Ыць аскунзь Фаца? Пентру че уйць де ненорочиря ши апэсаря ноастрэ?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
Кэч суфлетул не есте доборыт ын цэрынэ де мыхнире, трупул ностру есте липит де пэмынт.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Скоалэ-Те ка сэ не ажуць! Избэвеште-не, пентру бунэтатя Та!

< Masalimo 44 >