< Masalimo 44 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
MAIN Kot, je roner ki jalon at, jam at oko kajokajoi on kit er, me kom kotin wiadar ni ar anjau maj.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Kom kotin pakiweier men liki kan ki lim omui, ap wilian ir di; kom kotin koko jan wei kan, ap id katotoe ir ala.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
Pwe re jota kaloedier jap o ki ar kodlaj, o pa arail jota katepa on ir, pwe pali maun omui o lim omui, o marain en jilan omui; pweki kom kotin kupura irail er.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
Pwe komui Kot ai Nanmarki, me inauki on, Iakop, en jauaja i.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Komui, me je pan kawekila at imwintiti kan; ni mar omui me je pan tiakekidi me kin palian kit.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
Pwe i jota kin kaporoporeki ai kajik katieu, o ai kodlaj jota kak dore ia la.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
Pwe komui me kin jauaja kit jan at imwintiti kan, o kom kin kanamenokala, me kailon kin kit.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
Ran karoj je pan kapina Kot, o je pan danke on mar omui kokolata.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
Ari jo, kom kotin likidmalie kin kit ala, pwe jen lijela, o komui jota ian at karij akan.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Kom kotin mueid on at imwintiti, ren paki kit wei, o me kailon kin kit, kin kulia jan at kapwa.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Kom kotin mueid on ir, ren kawe kit ala dueta jip oko, o kom kotin kamueit kit pajan nan pun en men liki kan.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Kom netikila japwilim omui kan ni pwai jued, a komui ap jota kapwapwa kilar.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Kom kin kotin wiai on kit, jen kankaurur ren men imp at, o lalaue o jarodi ren me kapil kit pena.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Kom kotin wia kin kit karajepa eu ren men liki kan o aramaj akan kin duedualok kin kit.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
I kin jaro nin ran karoj o maj ai me dir en namenok,
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
Ni ai roneron aramaj morjued o lalaue, o ni ai kilekilan ai imwintiti o me kin akdepuk kan.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
Mepukat karoj lel don kit er, ari jo, je jota kak monokela komui, de wia dip on japwilim omui inau.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Monion at jota pupwei jan komui, o je jota wuki wei jan al omui.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
A komui kawe kit alar ni wajan man jued, o kom kadupale kidi mot en mela.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Ma je monokela mar en at Kol, o pokada pa at on amen kot,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
Kot jota pan kotin diarada? Pwe a kotin mani lol en monion at.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Pwe kit kin kalokoloke kin komui ni ran karoj, o kit rajon jip me pan kamela.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Main i, kom kotida! Da me kom kotin jaimokela? Kotin opada waja, o der kajapoke kit ala kolata!
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Da me kom kotin karirila jilan omui, o kotin maliela at luet o at kalokolok?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
Pwe nen it poridier ni pwel par; kaped it paj on pwel.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Kom kotida, jauaja kit, o dore kit ala pweki omui kalanan.