< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
Psalmus, filiis Core ad intellectum.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Deus auribus nostris audivimus: patres nostri annunciaverunt nobis. Opus, quod operatus es in diebus eorum: et in diebus antiquis.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
Manus tua gentes disperdidit, et plantasti eos: afflixisti populos, et expulisti eos:
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
Nec enim in gladio suo possederunt terram, et brachium eorum non salvavit eos: Sed dextera tua, et brachium tuum, et illuminatio vultus tui: quoniam complacuisti in eis.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Tu es ipse rex meus et Deus meus: qui mandas salutes Iacob.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
In te inimicos nostros ventilabimus cornu, et in nomine tuo spernemus insurgentes in nobis.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
Non enim in arcu meo sperabo: et gladius meus non salvabit me.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
Salvasti enim nos de affligentibus nos: et odientes nos confudisti.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
In Deo laudabimur tota die: et in nomine tuo confitebimur in saeculum.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Nunc autem repulisti et confudisti nos: et non egredieris Deus in virtutibus nostris.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Avertisti nos retrorsum post inimicos nostros: et qui oderunt nos, diripiebant sibi.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Dedisti nos tamquam oves escarum: et in gentibus dispersisti nos.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Vendidisti populum tuum sine pretio: et non fuit multitudo in commutationibus eorum.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Posuisti nos opprobrium vicinis nostris, subsannationem et derisum his, qui sunt in circuitu nostro.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
Posuisti nos in similitudinem Gentibus: commotionem capitis in populis.
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
Tota die verecundia mea contra me est, et confusio faciei meae cooperuit me.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
A voce exprobrantis, et obloquentis: a facie inimici, et persequentis.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Haec omnia venerunt super nos, nec obliti sumus te: et inique non egimus in testamento tuo.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
Et non recessit retro cor nostrum: et declinasti semitas nostras a via tua:
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Quoniam humiliasti nos in loco afflictionis, et cooperuit nos umbra mortis.
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
Si obliti sumus nomen Dei nostri, et si expandimus manus nostras ad deum alienum:
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Nonne Deus requiret ista? ipse enim novit abscondita cordis. Quoniam propter te mortificamur tota die: aestimati sumus sicut oves occisionis.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Exurge, quare obdormis Domine? exurge, et ne repellas in finem.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Quare faciem tuam avertis, oblivisceris inopiae nostrae et tribulationis nostrae?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
Quoniam humiliata est in pulvere anima nostra: conglutinatus est in terra venter noster.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Exurge Domine, adiuva nos: et redime nos propter nomen tuum.

< Masalimo 44 >