< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
Au chef de musique. Des fils de Coré. Instruction. Ô Dieu! nous avons entendu de nos oreilles, nos pères nous ont raconté l’œuvre que tu as opérée dans leurs jours, aux jours d’autrefois.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Tu as, par ta main, dépossédé les nations, et tu as planté nos pères; tu as affligé les peuples et tu les as chassés.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
Car ce n’est point par leur épée qu’ils ont possédé le pays, et ce n’est pas leur bras qui les a sauvés; car c’est ta droite et ton bras et la lumière de ta face, parce que tu avais pris ton plaisir en eux.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
C’est toi qui es mon roi, ô Dieu! Commande le salut pour Jacob.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Avec toi, nous frapperons nos adversaires; par ton nom, nous foulerons ceux qui s’élèvent contre nous.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
Car ce n’est pas en mon arc que je me confie, et mon épée ne me sauvera point;
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
Car tu nous as sauvés de nos adversaires, et tu rends confus ceux qui nous haïssent.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
En Dieu nous nous glorifierons tout le jour, et nous célébrerons ton nom à toujours. (Sélah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
Mais tu nous as rejetés et rendus confus, et tu ne sors plus avec nos armées;
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Tu nous as fait retourner en arrière devant l’adversaire, et ceux qui nous haïssent ont pillé pour eux-mêmes;
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Tu nous as livrés comme des brebis [destinées] à être mangées, et tu nous as dispersés parmi les nations;
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Tu as vendu ton peuple pour rien, et tu ne t’es pas agrandi par leur prix;
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Tu nous as mis en opprobre chez nos voisins, en risée et en raillerie auprès de nos alentours;
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Tu nous as mis comme proverbe parmi les nations, comme hochement de tête parmi les peuples.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
Tout le jour ma confusion est devant moi, et la honte de ma face m’a couvert,
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
À cause de la voix de celui qui outrage et qui injurie, à cause de l’ennemi et du vengeur.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
Tout cela nous est arrivé, et nous ne t’avons pas oublié, et nous n’avons pas été infidèles à ton alliance.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Notre cœur ne s’est pas retiré en arrière, et nos pas n’ont point dévié de ton sentier;
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
Quoique tu nous aies écrasés dans le lieu des chacals, et que tu nous aies couverts de l’ombre de la mort.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Si nous avions oublié le nom de notre Dieu, et étendu nos mains vers un dieu étranger,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
Dieu ne s’en enquerrait-il pas? car lui connaît les secrets du cœur.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Mais, à cause de toi, nous sommes mis à mort tous les jours, nous sommes estimés comme des brebis de tuerie.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Éveille-toi! Pourquoi dors-tu, Seigneur? Réveille-toi; ne nous rejette pas pour toujours.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Pourquoi caches-tu ta face, [et] oublies-tu notre affliction et notre oppression?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
Car notre âme est courbée jusque dans la poussière, notre ventre est attaché à la terre.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Lève-toi, aide-nous, et rachète-nous à cause de ta bonté.

< Masalimo 44 >