< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
to/for to conduct to/for son: descendant/people Korah Maskil God in/on/with ear our to hear: hear father our to recount to/for us work to work in/on/with day their in/on/with day front: old
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
you(m. s.) hand your nation to possess: take and to plant them be evil people and to send: let go them
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
for not in/on/with sword their to possess: take land: country/planet and arm their not to save to/for them for right your and arm your and light face your for to accept them
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
you(m. s.) he/she/it king my God to command salvation Jacob
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
in/on/with you enemy our to gore in/on/with name your to trample to arise: rise us
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
for not in/on/with bow my to trust and sword my not to save me
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
for to save us from enemy our and to hate us be ashamed
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
in/on/with God to boast: boast all [the] day: always and name your to/for forever: enduring to give thanks (Selah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
also to reject and be humiliated us and not to come out: come in/on/with army our
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
to return: return us back from enemy and to hate us to plunder to/for them
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
to give: make us like/as flock food and in/on/with nation to scatter us
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
to sell people your in/on/with not substance and not to multiply in/on/with price their
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
to set: make us reproach to/for neighboring our derision and derision to/for around us
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
to set: make us proverb in/on/with nation shaking head not people
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
all [the] day shame my before me and shame face my to cover me
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
from voice: sound to taunt and to blaspheme from face enemy and to avenge
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
all this to come (in): come us and not to forget you and not to deal in/on/with covenant your
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
not to turn back heart our and to stretch step our from way your
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
for to crush us in/on/with place jackal and to cover upon us in/on/with shadow
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
if to forget name God our and to spread palm our to/for god be a stranger
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
not God to search this for he/she/it to know secret heart
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
for upon you to kill all [the] day to devise: count like/as flock slaughtered
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
to rouse [emph?] to/for what? to sleep Lord to awake [emph?] not to reject to/for perpetuity
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
to/for what? face your to hide to forget affliction our and oppression our
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
for to sink to/for dust soul our to cleave to/for land: soil belly: abdomen our
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
to arise: rise [emph?] help to/for us and to ransom us because kindness your

< Masalimo 44 >