< Masalimo 44 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
For the leader. Of the Korahites. A maskil. O God, we have heard with our ears, all our ancestors have told us of the work that you wrought in their day, your wonders in days of old,
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
uprooting and crushing the nations, then planting and settling them. For it wasn’t their own sword that won them the land,
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
it was not their own arm that brought them the victory. Yours was the hand and the arm, yours was the face that shone on them with favor.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
It was you, my king and my God, that ordained the victories of Jacob.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Through you we can thrust back our foes, and by your name tread down our assailants:
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
for not in my bow do I trust, nor can my sword win me the victory.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
Our victory comes from you, and confusion to those who hate us.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
In God we boast all the day long, and your name will we praise forever. (Selah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
Yet you have spurned and disgraced us, in not going forth with our armies,
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
and in making us flee from the foe, so that those who hated us plundered us.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
You have let us be eaten like sheep, you have scattered us over the world,
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
sold your people for a pittance, and getting no gain from their price.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
You have made us the butt of our neighbors, the derision and scorn of all round us.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
O’er the world you have made us a byword, the nations at us shake their heads.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
My disgrace is forever before me, my face is covered with shame,
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
at the words of blasphemer and scoffer, at the sight of the foe and the vengeful.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
All this has come upon us, yet we have not forgotten you nor falsely dealt with your covenant.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Our heart has not turned back, nor our steps declined from your way,
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
that you thus should have crushed us down, and covered us over with gloom, in the place where the jackals roam.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Had we forgotten the name of our God, or stretched out our hands to a god that was strange,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
would God not have searched this out? For he knows the heart and its secrets.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
But in your cause it is we are killed all the day, and counted as sheep for the slaughter.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Rouse yourself, why do you sleep Lord? Awake, cast us not off forever.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Why do you hide your face, forgetting our stress and our misery?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
For we have sunk down to the dust, our bodies cling to the ground.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Arise, come to our help: for your love’s sake, ransom us.