< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
Unto the end. To the sons of Korah, toward understanding. We have heard, O God, with our own ears. Our fathers have announced to us the work that you wrought in their days and in the days of antiquity.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Your hand dispersed the Gentiles, and you transplanted them. You afflicted a people, and you expelled them.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
For they did not take possession of the land by their sword, and their own arm did not save them. But your right hand and your arm, and the light of your countenance did so, because you were pleased with them.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
You yourself are my king and my God, who commands the salvation of Jacob.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
With you, we will brandish a horn before our enemies; and in your name, we will spurn those rising up against us.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
For I will not hope in my bow, and my sword will not save me.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
For you have saved us from those who afflict us, and you have bewildered those who hate us.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
In God, we will give praise all day long; and in your name, we will confess forever.
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
But now, you have rejected and bewildered us, and you will not go forth with our armies, O God.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
You have turned our back to our enemies, and those who hated us have plundered for themselves.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
You have given us over like sheep for food. You have scattered us among the Gentiles.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
You have sold your people without a price, and no great number was exchanged for them.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
You have set us as a disgrace to our neighbors, a scoff and a derision to those who are around us.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
You have set us as a parable among the Gentiles, a shaking of the head among the peoples.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
All day long my shame is before me, and the confusion of my face has covered me,
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
before the voice of the reproacher and the commentator, before the face of the adversary and the pursuer.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
All these things have come upon us, yet we have not forgotten you, and we have not acted unjustly in your covenant.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
And our heart has not turned back. And you have not diverted our steps from your way.
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
For you humbled us in a place of affliction, and the shadow of death has covered us.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
If we have forgotten the name of our God, and if we have extended our hands to a foreign god,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
will not God find this out? For he knows the secrets of the heart.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
For, because of you, we are being killed all day long. We are considered as sheep for the slaughter.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Rise up. Why do you fall asleep, O Lord? Rise up, and do not reject us in the end.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Why do you turn your face away, and why do you forget our needfulness and our tribulation?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
For our soul has been humbled into the dust. Our belly has been bound to the earth.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Rise up, O Lord. Help us and redeem us, because of your name.

< Masalimo 44 >