< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
Přednímu zpěváku z synů Chóre, vyučující. Bože, ušima svýma slýchali jsme, a otcové naši vypravovali nám o skutcích, kteréž jsi činíval za dnů jejich, za dnů starodávních.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Tys sám rukou svou vyhnal pohany, a vštípil jsi je; potřel jsi lidi, a je jsi rozplodil.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
Neboť jsou neopanovali země mečem svým, aniž jim rámě jejich spomohlo, ale pravice tvá a rámě tvé, a světlost oblíčeje tvého, proto že jsi je zamiloval.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
Ty jsi sám král můj, ó Bože, udílejž hojného spasení Jákobova.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
V toběť jsme protivníky naše potírali, a ve jménu tvém pošlapávali jsme povstávající proti nám.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
Neboť jsem v lučišti svém naděje neskládal, aniž mne kdy obránil meč můj.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
Ale ty jsi nás vysvobozoval od nepřátel našich, a kteříž nás nenávidí, ty jsi zahanboval.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
A protož chválíme tě Boha na každý den, a jméno tvé ustavičně oslavujeme. (Sélah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
Ale nyní jsi nás zahnal i zahanbil, a nevycházíš s vojsky našimi.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Obrátil jsi nás nazpět, a ti, kteříž nás nenávidí, rozchvátali mezi sebou jmění naše.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Oddal jsi nás, jako ovce k snědení, i mezi pohany rozptýlil jsi nás.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Prodal jsi lid svůj bez peněz, a nenadsadils mzdy jejich.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Vydal jsi nás k utrhání sousedům našim, ku posměchu a ku potupě těm, kteříž jsou vůkol nás.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Uvedl jsi nás v přísloví mezi národy, a mezi lidmi, aby nad námi hlavou zmítáno bylo.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
Na každý den styděti se musím, a hanba tváři mé přikrývá mne,
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
A to z příčiny řeči utrhajícího a hanějícího, z příčiny nepřítele a vymstívajícího se.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
Všecko to přišlo na nás, a však jsme se nezapomenuli na tě, aniž jsme zrušili smlouvy tvé.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Neobrátilo se nazpět srdce naše, aniž se uchýlil krok náš od stezky tvé,
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
Ačkoli jsi nás byl potřel na místě draků, a přikryl jsi nás stínem smrti.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Kdybychom se byli zapomenuli na jméno Boha svého, a pozdvihli rukou svých k bohu cizímu,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
Zdaliž by toho Bůh byl nevyhledával? Nebo on zná skrytosti srdce.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Anobrž pro tebe mordováni býváme každého dne, jmíni jsme jako ovce k zabití oddané.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Procitiž, proč spíš, ó Pane? Probudiž se, a nezaháněj nás na věky.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
I pročež tvář svou skrýváš, a zapomínáš se na trápení a ssoužení naše?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
Nebotě se již sklonila až k prachu duše naše, přilnul k zemi život náš.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Povstaniž k našemu spomožení, a vykup nás pro své milosrdenství.

< Masalimo 44 >