< Masalimo 43 >
1 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
God, deme thou me, and departe thou my cause fro a folc not hooli; delyuere thou me fro a wickid man, and gileful.
2 Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
For thou art God, my strengthe; whi hast thou put me abac, and whi go Y soreuful, while the enemy turmentith me?
3 Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
Sende out thi liyt, and thi treuthe; tho ledden me forth, and brouyten in to thin hooli hil, and in to thi tabernaclis.
4 Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
And Y schal entre to the auter of God; to God, that gladith my yongthe. God, my God, Y schal knowleche to thee in an harpe; my soule,
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.
whi art thou sory, and whi troblist thou me? Hope thou in God, for yit Y schal knouleche to hym; he is the helthe of my cheer, and my God.