< Masalimo 43 >
1 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
Suď mne, ó Bože, a zasaď se o mou při; od národu nemilosrdného, a od člověka lstivého a nepravého vytrhni mne.
2 Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
Nebo ty jsi Bůh mé síly. Proč jsi mne zapudil? Proč pro ssoužení od nepřítele v smutku mám ustavičně choditi?
3 Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
Sešliž světlo své a pravdu svou, to ať mne vodí a zprovodí na horu svatosti tvé a do příbytků tvých,
4 Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
Abych přistoupil k oltáři Božímu, k Bohu radostného plésání mého, a budu tě oslavovati na harfě, ó Bože, Bože můj.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.
Proč jsi smutná, duše má, a proč se kormoutíš ve mně? Posečkej na Boha, neboť ještě vyznávati jej budu; onť jest hojné spasení tváři mé a Bůh můj.