< Masalimo 42 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
Kumqondisi wokuhlabela. Ihubo lamaDodana kaKhora. Njengempala inxwanela imifula yamanzi, kunjalo umphefumulo wami uyakunxwanela, Oh Nkulunkulu.
2 Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
Umphefumulo wami womela uNkulunkulu, uNkulunkulu ophilayo. Ngizahamba nini ngiyohlangana loNkulunkulu?
3 Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Inyembezi zami seziyikudla kwami imini lobusuku, lapho abantu besithi kimi ilanga lonke, “Ungaphi uNkulunkulu wakho?”
4 Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
Lezizinto ngiyazikhumbula nxa ngizisola kakhulu ngidabukile: Ngangihamba endlini kaNkulunkulu, ngaphansi kwempiko zikaSomandla sihlokoma ngentokozo langokubonga lexuku elithakazelela umkhosi.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
Kungani wephukile na, wena mphefumulo wami? Kungani udungekile kanje ngaphakathi kwami? Beka ithemba lakho kuNkulunkulu, ngoba ngisezakumdumisa, uMsindisi wami loNkulunkulu wami.
6 Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
Umphefumulo wami wephukile ngaphakathi kwami; ngakho ngizakukhumbula kusukela esifundeni seJodani, iziqongo zaseHemoni, kusukela entabeni iMizari.
7 Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
Inziki imemeza inziki phakathi kwenhlokomo yezimpophoma zakho; wonke amavinqo lokukhaphaka sekugabhela phezu kwami.
8 Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
Emini uThixo uyaluqondisa uthando lwakhe ebusuku ingoma yakhe ikhona kimi umkhuleko kuNkulunkulu wempilo yami.
9 Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
Ngithi kuNkulunkulu iDwala lami, “Kutheni usungikhohliwe na? Kutheni sengizula ngingolilayo, ngincindezelwa yisitha na?”
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Amathambo ami ezwa ubuhlungu obungiqedayo lapho izitha zami zingihoza, zisithi kimi ilanga lonke, “Ungaphi uNkulunkulu wakho?”
11 Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
Kungani wephukile na, wena mphefumulo wami? Kungani udungekile kanje ngaphakathi kwami? Beka ithemba lakho kuNkulunkulu, ngoba ngisezakumdumisa, uMsindisi wami loNkulunkulu wami.