< Masalimo 42 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
Manahake ty fisehasehàn-temboay an-torahañe mitsiritsioke ty fisañasañan-troko ama’o ry Andrianañahare.
2 Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
Iheaheàn-troko t’i Andrianañahare, i Andrianañahare veloñey; ombia ty hombako hiheo mb’añatrefan’Añahare mb’eo?
3 Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Filintsako handro an-kale, o ranomasokoo, ie kizaheñe ­lomoñandro, ami’ty hoe: Aia ze o Andrianañahare’o zao?
4 Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
Tiahiko o raha zao, le haborako ty an-troko ao, ie nindrezako lia i màroy, ninday iareo nangovovoke mb’añ’anjomban’ Añahare mb’eo, am-peom-pirebehañe naho fandrengeañe, i lahialeñe mitañ’andro nifotoañeñey
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
Ino ty ilonjera’o ry fiaiko? ino ty ikoreokoreoha’o añ’ovako ao? Mitama an’Andrianañahare; fa mbe ho andriañe’o, ty ­fandrombahañe añ’atrefa’o.
6 Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
Ry Andrianañahareko, Mitsilofìñe añ’ovako ao ty troko, tiahiko irehe boak’ an-tane Iordane ao, naho an-dengo’ i Kermone eñe, hirik’am-bohi-Mitsarey añe.
7 Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
Tokave’ i lalekey ty laleke ami’ty fitroña’ o kinera’eo. songa mandipotse ahy o onja naho ren-drano’oo.
8 Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
Hafanto’ Iehovà an-kandro ty fiferenaiña’e, le amako an-kaleñe i sabo’ey, ty halaliko aman’ Añaharen-kaveloko.
9 Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
Hoe iraho aman’ Añahare lamilamiko: Akore ty nandikofa’o ahiko? Ino ty andalàko ty famorekekèan- drafelahy?
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Hoe ­fañotohotoañe ty an-taolako ao, ty fiteraterà’ o rafelahikoo; ie anoa’e ty hoe lomoñandro, Aia ze o Andrianañahare’o zao?
11 Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
Ino ty ilonjera’o, ty troko tia? Ino ty ­fivalitsikotahañe añ’ovako ao? Mitamà an’Andrianañahare; fa mbe handriañe’o i fandrombahan-tareheko naho Andrianañaharekoy.

< Masalimo 42 >