< Masalimo 42 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
За първия певец. Поучение за Кореевите синове. Както еленът пъхти за водните потоци, Така душата ми въздиша за Тебе, Боже.
2 Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
Жадна е душата ми за Бога, за живия Бог; Кога ще дойда и ще се явя пред Бога?
3 Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Моите сълзи ми станаха храна денем и нощем, Като непрестанно ми думат: Где е твоят Бог?
4 Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
Изливам душата си дълбоко в мене като си напомням това, - Как отивах с множеството, И завеждах шествието в Божия дом С глас на радост и на хваление, С множеството, което празнуваше.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
Защо си отпаднала душо моя? И защо се смущаваш дълбоко в мене? Надявай се на Бога: защото аз още ще Го славословя За помощта от лицето Му.
6 Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
Боже мой, душата ми е отпаднала дълбоко в мене; Затова си спомням за Тебе от земята на Иордана И на планините Ермон, от гората Мисар.
7 Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
Бездна призовава бездна с шума на Твоите водопади; Всичките Твои вълни и Твои развълнувани води преминаха над мене;
8 Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
Но пак денем Господ ще заръча за мене милостта Си, И нощем песента Му ще бъде с мене И молитвата към Бога на живота ми.
9 Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
Ще река на Бога, моята канара: Защо си ме забравил? Защо ходя нажалан поради притеснението от неприятеля?
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Като със смазване на костите ми противниците ми ме укоряват, И непрестанно ми думат: Где е твоят Бог?
11 Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
Защо си отпаднала, душо моя? И защо се смущаваш дълбоко в мене? Надявай се на Бога; аз още ще славословя: Той е помощ на лицето ми и Бог мой.

< Masalimo 42 >