< Masalimo 41 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
¡Oh cuán bendecido es el que piensa en el pobre! En el día malo Yavé lo librará.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
Yavé lo protegerá y le dará vida. Será bendito en la tierra, Y no lo entregarás a la voluntad de sus enemigos.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
Yavé lo sustentará en el lecho de dolor. En su enfermedad suavizarás su cama.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
Dije yo: Oh Yavé, ten compasión de mí. Sana mi alma, porque pequé contra Ti.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Mis enemigos hablan mal de mí y preguntan: ¿Cuándo morirá y perecerá su nombre?
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
Cuando viene a verme, habla falsedad. Su corazón recoge perversidades. Cuando sale las divulga.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
Todos los que me aborrecen murmuran reunidos contra mí. Maquinan la perversidad contra mí y dicen:
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
Algo perverso fue derramado sobre él. Cuando caiga en cama, no volverá a levantarse.
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Aun el hombre de mi paz en quien yo confiaba, Que comía de mi pan, Levantó contra mí su talón.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
Pero Tú, oh Yavé, ten compasión de mí. Levántame para que le dé recompensa.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
En esto sé que te complaces en mí: En que mi enemigo no proclame triunfo sobre mí.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
En cuanto a mí, en mi integridad me sostienes, Y me establecerás en tu Presencia para siempre.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
¡Bendito sea Yavé el ʼElohim de Israel, Desde la eternidad y hasta la eternidad! ¡Amén y amén!