< Masalimo 41 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
Ubusisiwe onanzelela obuthakathaka. INkosi izamkhulula ngosuku lobubi.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
INkosi izamlondoloza, imgcine ephila; uzabusiswa emhlabeni; kawuyikumnikela entandweni yezitha zakhe.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
INkosi izamsekela embhedeni wokugula kwakhe; wena uzaguqula lonke icansi lakhe emkhuhlaneni wakhe.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
Mina ngathi: Nkosi, woba lomusa kimi, silisa umphefumulo wami, ngoba ngonile kuwe.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Izitha zami zikhuluma okubi ngami zisithi: Uzakufa nini, lebizo lakhe lichitheke?
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
Lalapho efika ukungibona, ukhuluma inkohliso; inhliziyo yakhe izibuthela okubi, esephumile phandle akhulume.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
Bonke abangizondayo banyenyezelana bemelene lami, bangisongele ukungona.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
Into embi inamathele kuye; njalo njengoba elele phansi kasayikuvuka.
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Yebo, indoda yobungane bami engiyithembayo, ebikade isidla isinkwa sami, ingiphakamisele isithende imelene lami.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
Kodwa, wena Nkosi, woba lomusa kimi, ungilulamise ukuze ngibaphindisele.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
Ngalokhu ngiyazi ukuthi uyangithanda, ngoba isitha sami kasithabanga phezu kwami.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
Kodwa mina, ungisekele ebuqothweni bami, wangimisa phambi kwakho kuze kube nininini.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Kayibongwe iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, kusukela phakade kuze kube phakade. Ameni, loAmeni.

< Masalimo 41 >