< Masalimo 41 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
Psalmus David, in finem. Beatus vir qui intelligit super egenum, et pauperem: in die mala liberabit eum Dominus.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
Dominus conservet eum, et vivificet eum, et beatum faciat eum in terra: et non tradat eum in animam inimicorum eius.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
Dominus opem ferat illi super lectum doloris eius: universum stratum eius versasti in infirmitate eius.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
Ego dixi: Domine miserere mei: sana animam meam, quia peccavi tibi.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Inimici mei dixerunt mala mihi: Quando morietur, et peribit nomen eius?
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
Et si ingrediebatur ut videret, vana loquebatur, cor eius congregavit iniquitatem sibi. Egrediebatur foras, et loquebatur
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
in idipsum. Adversum me susurrabant omnes inimici mei: adversum me cogitabant mala mihi.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
Verbum iniquum constituerunt adversum me: Numquid qui dormit non adiiciet ut resurgat?
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Etenim homo pacis meae, in quo speravi: qui edebat panes meos, magnificavit super me supplantationem.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
Tu autem Domine miserere mei, et resuscita me: et retribuam eis.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
In hoc cognovi quoniam voluisti me: quoniam non gaudebit inimicus meus super me.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
Me autem propter innocentiam suscepisti: et confirmasti me in conspectu tuo in aeternum.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Benedictus Dominus Deus Israel a saeculo, et usque in saeculum: fiat, fiat.

< Masalimo 41 >