< Masalimo 41 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
“For the leader of the music. A psalm of David.” Happy is he who hath regard to the poor! The LORD will deliver him in time of trouble.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
The LORD will preserve him, and keep him alive; He shall be happy on the earth; Thou wilt not give him up to the will of his enemies!
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
The LORD will strengthen him upon the bed of disease; All his bed thou wilt change in his sickness.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
I said, O LORD! be merciful to me! Heal me, for I have sinned against thee!
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
My enemies speak evil of me: “When will he die, and his name perish?”
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
If one come to see me, he speaketh falsehood; His heart gathereth malice; When he goeth abroad, he uttereth it.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
All that hate me whisper together against me; Against me do they devise mischief:
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
“A deadly disease cleaveth fast unto him; He lieth down, and he shall never arise!”
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Yea, my familiar friend in whom I trusted, who did eat of my bread, —He hath lifted up his heel against me.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
But do thou, O LORD! have pity upon me; Raise me up, that I may requite them!
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
By this I know that thou favorest me, Because my enemy doth not triumph over me.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
As for me, thou wilt uphold me in my integrity; Thou wilt set me before thy face for ever!
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
[Praised be Jehovah, the God of Israel, From everlasting to everlasting. Amen! Amen!]

< Masalimo 41 >