< Masalimo 41 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
[For the Chief Musician. A Psalm by David.] Blessed is he who considers the poor and needy. Jehovah will deliver him in the day of evil.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
Jehovah will protect him, and keep him alive. He shall be blessed on the earth, and he will not surrender him to the will of his enemies.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
Jehovah will sustain him on his sickbed, and restore him from his bed of illness.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
I said, "Jehovah, have mercy on me. Heal me, for I have sinned against you."
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
My enemies speak evil against me: "When will he die, and his name perish?"
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
If he comes to see me, he speaks falsehood. His heart gathers iniquity to itself. When he goes abroad, he tells it.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
All who hate me whisper together against me. They imagine the worst for me.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
"A wicked thing is poured out on him; and he who lies down will not rise again."
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Even my own close friend, in whom I trusted, who ate my bread, has lifted up his heel against me.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
But you, Jehovah, have mercy on me, and raise me up, that I may repay them.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
By this I know that you delight in me, because my enemy doesn't triumph over me.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
As for me, you uphold me in my integrity, and set me in your presence forever.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Blessed be Jehovah, the God of Israel, from everlasting and to everlasting. Amen and amen.

< Masalimo 41 >