< Masalimo 41 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
To him that excelleth. A Psalme of Dauid. Blessed is he that iudgeth wisely of the poore: the Lord shall deliuer him in ye time of trouble.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
The Lord will keepe him, and preserue him aliue: he shalbe blessed vpon the earth, and thou wilt not deliuer him vnto the will of his enemies.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
The Lord wil strengthen him vpon ye bed of sorow: thou hast turned al his bed in his sicknes.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
Therefore I saide, Lord haue mercie vpon me: heale my soule, for I haue sinned against thee.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Mine enemies speake euill of me, saying, When shall he die, and his name perish?
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
And if hee come to see mee, hee speaketh lies, but his heart heapeth iniquitie within him, and when he commeth foorth, he telleth it.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
All they that hate me, whisper together against me: euen against me do they imagine mine hurt.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
A mischiefe is light vpon him, and he that lyeth, shall no more rise.
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Yea, my familiar friend, whom I trusted, which did eate of my bread, hath lifted vp the heele against me.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
Therefore, O Lord, haue mercy vpon mee, and raise me vp: so I shall reward them.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
By this I know that thou fauourest me, because mine enemie doth not triumph against me.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
And as for me, thou vpholdest me in mine integritie, and doest set me before thy face for euer.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Blessed be the Lord God of Israel worlde without ende. So be it, euen so be it.