< Masalimo 41 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
For the end, a Psalm of David. Blessed [is the man] who thinks, on the poor and needy: the Lord shall deliver him in an evil day.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
May the Lord preserve him and keep him alive, and bless him on the earth, and not deliver him into the hands of his enemy.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
May the Lord help him upon the bed of his pain; you have made all his bed in his sickness.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
I said, O Lord, have mercy upon me; heal my soul; for I have sinned against you.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Mine enemies have spoken evil against me, [saying], When shall he die, and his name perish?
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
And if he came to see [me], his heart spoke vainly; he gathered iniquity to himself; he went forth and spoke in like manner.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
All my enemies whispered against me; against me they devised my hurt.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
They denounced a wicked word against me, [saying], Now that he lies, shall he not rise up again?
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
For even the man of my peace, in whom I trusted, who ate my bread, lifted up [his] heel against me.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
But you, O Lord, have compassion upon me, and raise me up, and I shall requite them.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
By this I know that you have delighted in me, because mine enemy shall not rejoice over me.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
But you did help me because of [mine] innocence, and have established me before you for ever.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Blessed [be] the Lord God of Israel from everlasting, and to everlasting. So be it, so be it.

< Masalimo 41 >