< Masalimo 41 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
Zborovođi. Psalam. Davidov. Blago onome koji misli na uboga i slaba: u dan nevolje Jahve će ga spasiti!
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
Jahve će ga štititi i živa sačuvati, sreću mu dati na zemlji i neće ga predati na volju dušmanima.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
Jahve će ga ukrijepiti na postelji boli, bolest mu okrenuti u snagu.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
Zavapih: “Jahve, smiluj mi se, iscijeli mi dušu jer tebi sagriješih!”
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Neprijatelji zlo govore o meni: “Kad će umrijeti i kad će mu nestati imena?”
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
I dođe li tko da me posjeti, himbeno govori, u srcu pakosti skuplja i vani opada.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
Mrzitelji moji svi složno šapuću o meni; zlo mi dosuđuju:
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
“Pogubna se pošast na nj oborila.” Ili: “Tko jednom leže, više ne ustaje.”
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Pa i prijatelj moj u koga se uzdah, koji blagovaše kruh moj, petu na me podiže.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
A ti, Jahve, smiluj se meni i podigni me da im mogu uzvratiti.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
Po tome ću znati da sam mio tebi: što se dušmanin moj neće veseliti nada mnom.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
A mene ćeš zdrava uzdržati i pred svoje me lice staviti dovijeka.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Blagoslovljen Jahve, Bog Izraelov, od vijeka do vijeka! Tako neka bude! Amen!