< Masalimo 41 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
Kathutkung: Devit Tamimathoe hanelah ka pouk pouh e tami teh a yawkahawi e doeh. Runae tueng nah ahni hah BAWIPA ni a hlout sak han.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
BAWIPA ni a hlout sak vaiteh, a pasai han. A tarannaw koe poe hanlah na pasoung mahoeh.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
A pataw teh sut a yan navah BAWIPA ni thapoe vaiteh, amae hmalah bout na thaw sak han.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
BAWIPA na pahren haw, ka hringnae heh dam sak haw. Bangkongtetpawiteh, nang taranlahoi ka yon toe telah ka ti.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Ka tarannaw ni nâtuek maw a due vaiteh a min raphoe lah ao han telah, thoenae koelah dueng na dei awh.
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
Na tho sin nahaiyah laithoe duengdoeh a dei awh. A lungthin ni payonnae dueng hah a pâkhueng teh, alawilah a tâco nah tangkuem koe ouk a dei.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
Na kahmuhmanaw pueng ni kai taranlahoi arulawk a kâdei awh teh, kai pataw nahane dueng doeh a kâdei awh.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
Patawnae kathout ni a man toung dawkvah, atu sut a yan toe, thaw mahoeh toe telah a kâdei awh.
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Ka hui kahawi, ka kâuep e, kaie rawca ka cat e niyah, kai taranlahoi a khokpaimai na tawm sin.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
Hatei, Oe BAWIPA, ahnimouh moi ka pathung thai nahanlah, na pahren nateh, bout na thaw sak haw.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
Hete kong dawk kai dawk na lunghawi doeh tie ka panue. Bangkongtetpawiteh, ka tarannaw ni na tâ awh hoeh.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
Kai teh pouknae kalan ka tawn dawkvah, na tawm nateh na hmalah pou na hrueng haw.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Isarel BAWIPA teh, a yungyoe hoi a yungyoe totouh pholen lah awm lawiseh. Amen hoi Amen.