< Masalimo 40 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mofatsa ndinadikira Yehova Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
Dāvida dziesma. Dziedātāju vadonim. Es gaidu gaidīdams uz To Kungu, Viņš griežas pie manis un paklausa manu kliegšanu.
2 Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko, mʼthope ndi mʼchithaphwi; Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
Jo Viņš mani izvilka no briesmīgas bedres un no dubļainām dūņām un cēla manas kājas uz akmens kalnu un stiprināja manus soļus.
3 Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga, nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga. Ambiri adzaona, nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.
Un ir licis manā mutē jaunu dziesmu, teikšanas dziesmu mūsu Dievam; daudzi to redzēs un bīsies un cerēs uz To Kungu.
4 Ndi wodala munthu amakhulupirira Yehova; amene sayembekezera kwa odzikuza, kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Svētīgs tas vīrs, kas savu cerību liek uz To Kungu, un negriežās pie tiem lepniem un pie tiem, kas ar meliem tinās.
5 Zambiri, Yehova Mulungu wanga, ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita. Zinthu zimene munazikonzera ife palibe amene angathe kukuwerengerani. Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera, zidzakhala zambiri kuzifotokoza.
Kungs, mans Dievs, lieli ir Tavi brīnumi, ko Tu mums parādi, un Tavi padomi; nekas Tev nav līdzinājams. Es tos gribu pasludināt un izteikt, tie nav izskaitāmi.
6 Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna, koma makutu anga mwawatsekula; zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo Inu simunazipemphe.
Upuri un ēdami upuri Tev nepatīk, ausis Tu man esi atvēris; dedzināmos upurus un grēku upurus Tu neprasi.
7 Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera. Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Tad es sacīju: Redzi, es nāku, grāmatā stāv par mani rakstīts.
8 Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga; lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
Man ir prieks, darīt Tavu prātu, mans Dievs, un Tava bauslība ir manā sirds dziļumā.
9 Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu; sinditseka milomo yanga monga mukudziwa Inu Yehova.
Es sludināšu taisnību lielā draudzē; redzi, savas lūpas es neaizdarīšu; Kungs, Tu to zini.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga; ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu. Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu pa msonkhano waukulu.
Tavu taisnību es neslēpju savā sirdī, no Tavas patiesības un pestīšanas es runāju, Tavu žēlastību un uzticību es neslēpju lielā draudzē.
11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova; chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
Tu, ak Kungs, nenovērs Savu apžēlošanu no manis; lai Tava žēlastība un patiesība vienmēr mani pasargā!
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira; machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona. Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga, ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
Jo ap mani ir apmetušās bēdas, ko nevar skaitīt, mani noziegumi mani sagrābuši, ka nevaru redzēt; viņu ir vairāk, nekā matu uz manas galvas, un mana sirds mani atstājusi.
13 Pulumutseni Yehova; Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
Lai tev patīk, Kungs, mani izglābt, steidzies, ak Kungs, man palīgā!
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene amakhumba chiwonongeko changa abwezedwe mwamanyazi.
Lai top kaunā un kopā paliek par apsmieklu, kas manu dvēseli meklē, to samaitāt; lai top dzīti atpakaļ un paliek kaunā, kas par manu nelaimi priecājās!
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!” abwerere akuchita manyazi.
Lai savas bezkaunības dēļ tie iztrūcinājās, kas no manis saka: tā, tā.
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
Lai priecājās un līksmojās iekš Tevis visi, kas Tevi meklē, un lai tie, kas Tavu pestīšanu mīļo, allažiņ saka: Tas Kungs ir augsti teicams.
17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa; Ambuye andiganizire. Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga; Inu Mulungu wanga, musachedwe.
Gan es esmu bēdīgs un nabags, bet Tas Kungs par mani gādā. Tu esi mans palīgs un mans glābējs; ak, mans Dievs, nekavējies!