< Masalimo 40 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mofatsa ndinadikira Yehova Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
Au chef des chantres; de David. Psaume. J’Ai placé mon ferme espoir en l’Eternel: il s’est incliné vers moi, il a entendu ma supplication.
2 Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko, mʼthope ndi mʼchithaphwi; Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
Il m’a retiré d’un gouffre tumultueux, d’un bourbier fangeux; il a posé mes pieds sur le roc et affermi mes pas.
3 Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga, nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga. Ambiri adzaona, nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.
Il a mis dans ma bouche un cantique nouveau, des louanges en l’honneur de notre Dieu; beaucoup s’en aperçoivent, éprouvent de la vénération, et mettent leur confiance en l’Eternel.
4 Ndi wodala munthu amakhulupirira Yehova; amene sayembekezera kwa odzikuza, kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Heureux l’homme qui cherche sa sécurité en l’Eternel, et ne se tourne pas vers les orgueilleux et les amis du mensonge!
5 Zambiri, Yehova Mulungu wanga, ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita. Zinthu zimene munazikonzera ife palibe amene angathe kukuwerengerani. Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera, zidzakhala zambiri kuzifotokoza.
Que de prodiges, ô Eternel, mon Dieu, que de desseins tu as accomplis en notre faveur! Rien n’est comparable à toi, j’aimerais les proclamer et les redire encore… Leur grand nombre défie toute description.
6 Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna, koma makutu anga mwawatsekula; zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo Inu simunazipemphe.
Tu ne souhaites ni sacrifice ni oblation, tu m’as perforé des oreilles pour entendre tu n’exiges ni holocaustes ni expiatoires.
7 Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera. Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Aussi je dis: "Voici, je me présente! Dans le rouleau du livre se trouve ce qui m’est prescrit.
8 Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga; lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
Accomplir ta volonté, mon Dieu, tel est mon désir; ta loi a pénétré jusqu’au fond de mes entrailles."
9 Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu; sinditseka milomo yanga monga mukudziwa Inu Yehova.
J’Ai proclamé ton équité dans une nombreuse assemblée, voici, je n’ai pas tenu mes lèvres closes: Eternel, toi, tu le sais.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga; ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu. Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu pa msonkhano waukulu.
Je n’ai point fait le silence sur ta justice, dont mon cœur est plein; j’ai dit ta fidélité et ta protection; je n’ai point caché ta grâce et ta bienveillance à la grande foule.
11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova; chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
Toi, non plus, ne me refuse pas ta clémence; que ta grâce et ta bonté me protègent sans cesse!
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira; machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona. Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga, ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
car des maux sans nombre m’assiègent, mes péchés m’ont débordé, je ne puis plus rien voir; ils sont plus abondants que les cheveux de ma tête; aussi mon cœur est-il défaillant en moi.
13 Pulumutseni Yehova; Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
Consens, Seigneur, à me sauver; Eternel, hâte-toi de me porter secours.
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene amakhumba chiwonongeko changa abwezedwe mwamanyazi.
Qu’ils soient ensemble confondus et couverts de honte, ceux qui attentent à ma vie, pour la supprimer! Qu’ils lâchent pied et reculent, en rougissant, ceux qui souhaitent mon malheur!
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!” abwerere akuchita manyazi.
Qu’ils soient frappés de stupeur par suite de leur honte, ceux qui disent de moi: "Ha! Ha!"
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
Mais qu’ils jubilent et se réjouissent en toi, tous ceux qui te recherchent; qu’ils disent constamment: "Dieu est grand!" ceux qui aiment ta protection!
17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa; Ambuye andiganizire. Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga; Inu Mulungu wanga, musachedwe.
Quant à moi, pauvre et malheureux, que mon Seigneur ait égard à moi! Tu es mon aide et ma sauvegarde: Eternel, n’attends pas trop longtemps.

< Masalimo 40 >