< Masalimo 40 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mofatsa ndinadikira Yehova Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
“For the leader of the music. A psalm of David.” I trusted steadfastly in the LORD, And he listened, and heard my cry.
2 Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko, mʼthope ndi mʼchithaphwi; Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
He drew me out of a horrible pit, Out of the miry clay; He set my feet upon a rock, And made my steps firm.
3 Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga, nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga. Ambiri adzaona, nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.
He hath put into my mouth a new song, A song of praise to our God. Many shall see, and fear, And put their trust in the LORD.
4 Ndi wodala munthu amakhulupirira Yehova; amene sayembekezera kwa odzikuza, kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Happy the man who maketh the LORD his trust, And resorteth not to men of pride and falsehood!
5 Zambiri, Yehova Mulungu wanga, ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita. Zinthu zimene munazikonzera ife palibe amene angathe kukuwerengerani. Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera, zidzakhala zambiri kuzifotokoza.
Many, O LORD, my God! are the wonderful works which thou hast done; Many have been thy gracious purposes towards us; None can be compared to thee! Would I declare and rehearse them, they are more than can be numbered.
6 Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna, koma makutu anga mwawatsekula; zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo Inu simunazipemphe.
In sacrifice and oblation thou hast no pleasure; Mine ears thou hast opened; Burnt-offering and sin-offering thou requirest not.
7 Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera. Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Therefore I said, “Lo, I come; In the scroll of the book it is prescribed to me;
8 Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga; lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
O my God! to do thy will is my delight, And thy law dwelleth in my heart!”
9 Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu; sinditseka milomo yanga monga mukudziwa Inu Yehova.
I have proclaimed thy righteousness in the great assembly; Lo, I have not restrained my lips, O LORD! thou knowest!
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga; ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu. Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu pa msonkhano waukulu.
I hide not thy justice in my heart; I declare thy faithfulness and thy salvation; I conceal not thy mercy and truth from the great assembly.
11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova; chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
Withdraw not from me thy tender mercies, O LORD! May thy loving-kindness and thy truth continually preserve me!
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira; machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona. Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga, ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
For evils without number have encompassed me; My iniquities have overtaken me; I cannot see the end of them; They are more than the hairs of my head, And my heart dieth within me.
13 Pulumutseni Yehova; Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
May it please thee, O LORD! to deliver me! O LORD! make haste to mine aid!
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene amakhumba chiwonongeko changa abwezedwe mwamanyazi.
May they all be confounded and covered with shame Who seek to take away my life! Let them be driven back with disgrace Who desire to do me injury!
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!” abwerere akuchita manyazi.
Let them be overwhelmed with confusion Who cry out to me, Aha! aha!
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
But let all who seek thee Be glad and rejoice in thee! Let those who love thy protection Ever say, “Great is Jehovah!”
17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa; Ambuye andiganizire. Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga; Inu Mulungu wanga, musachedwe.
I am poor and afflicted, yet the Lord thinketh upon me; Thou art my help and my deliverer; My God! make no delay!

< Masalimo 40 >