< Masalimo 4 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
[For the Chief Musician; on stringed instruments. A Psalm by David.] Answer me when I call, God of my righteousness. You set me free in my distress. Be gracious to me and hear my prayer.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
You sons of man, how long will you shame my honor, love what is worthless, chase after a lie? (Selah)
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
But know that the LORD works wonders for his godly one; the LORD will hear when I call to him.
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Be angry, but do not sin. Ponder in your heart, but be at rest on your bed. (Selah)
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Offer the sacrifices of righteousness, and put your trust in the LORD.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
Many say, "Who will show us any good?" LORD, lift up the light of your face upon us.
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
You have put gladness in my heart, more than when their grain and wine and oil abound.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
In peace I will both lay myself down and sleep, for you alone, LORD, make me live in safety.

< Masalimo 4 >