< Masalimo 4 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
“To the chief musician on Neginoth, a psalm of David.” When I call, answer me, O God of my righteousness: amidst distress thou hast [ever] granted me enlargement; be gracious unto me, and hear my prayer.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
O ye sons of men, how long shall my glory be put to shame? [how long] will ye love vanity, will ye seek for lies? (Selah)
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
But know that the Lord hath set apart the pious for himself: the Lord will hear when I call on him.
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Tremble, and sin not: commune with your heart upon your bed, and be still (Selah)
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Offer the sacrifices of righteousness, and put your trust in the Lord.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
Many say, “Who will show us happiness? Let shine brightly over us the light of thy countenance, O Lord.”
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
[But] thou hast placed more joy in my heart than at the time when their corn and their wine were increased.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
In peace, altogether, will I lay me down and sleep; for thou, Lord, alone, causest me to dwell in safety.