< Masalimo 4 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
HEAR me when I call, O God of my righteousness: thou hast enlarged me when I was in distress; have mercy upon me, and hear my prayer.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
O ye sons of men, how long will ye turn my glory into shame? how long will ye love vanity, and seek after leasing? (Selah)
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
But know that the Lord hath set apart him that is godly for himself: the Lord will hear when I call unto him.
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Stand in awe, and sin not: commune with your own heart upon your bed, and be still. (Selah)
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Offer the sacrifices of righteousness, and put your trust in the Lord.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
There be many that say, Who will shew us any good? Lord, lift thou up the light of thy countenance upon us.
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
Thou hast put gladness in my heart, more than in the time that their corn and their wine increased.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
I will both lay me down in peace, and sleep: for thou, Lord, only makest me dwell in safety.