< Masalimo 4 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
In parts according to verses. A Psalm of David. When I called upon him, the God of my justice heeded me. In tribulation, you have enlarged me. Have mercy on me, and heed my prayer.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
Sons of men, how long will you be dull in heart, so that whatever you love is in vain, and whatever you seek is false? (Pause)
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
And know this: the Lord has made wondrous his holy one. The Lord will heed me when I cry out to him.
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Be angry, and do not be willing to sin. The things that you say in your hearts: be sorry for them on your beds. (Pause)
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Offer the sacrifice of justice, and hope in the Lord. Many say, “Who reveals to us what is good?”
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
The light of your countenance, Lord, has been sealed upon us. You have given joy to my heart.
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
By the fruit of their grain, wine, and oil, they have been multiplied.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
In peace itself, I will sleep and I will rest. For you, O Lord, have established me singularly in hope.

< Masalimo 4 >