< Masalimo 4 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
For the choirmaster. With stringed instruments. A Psalm of David. Answer me when I call, O God of my righteousness! You have relieved my distress; show me grace and hear my prayer.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
How long, O men, will my honor be maligned? How long will you love vanity and seek after lies?
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
Know that the LORD has set apart the godly for Himself; the LORD hears when I call to Him.
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Be angry, yet do not sin; on your bed, search your heart and be still.
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Offer the sacrifices of the righteous and trust in the LORD.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
Many ask, “Who can show us the good?” Shine the light of Your face upon us, O LORD.
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
You have filled my heart with more joy than when grain and new wine abound.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
I will lie down and sleep in peace, for You alone, O LORD, make me dwell in safety.

< Masalimo 4 >