< Masalimo 39 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
Зичям: „Вой вегя асупра кэилор меле, ка сэ ну пэкэтуеск ку лимба; ымь вой пуне фрыу гурий кыт ва ста чел рэу ынаинтя мя.”
2 Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
Ам стат мут, ын тэчере; ам тэкут, мэкар кэ ерам ненорочит, ши тотушь дуреря мя ну ера май пуцин маре.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
Ымь ардя инима ын мине, ун фок лэунтрик мэ мистуя, ши атунч мь-а венит кувынтул пе лимбэ ши ам зис:
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
„Доамне, спуне-мь каре есте сфыршитул веций меле, каре есте мэсура зилелор меле, ка сэ штиу кыт де трекэтор сунт!”
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
Ятэ кэ зилеле меле сунт кыт ун лат де мынэ ши вяца мя есте ка о нимика ынаинтя Та. Да, орьче ом есте доар о суфларе, орькыт де бине с-ар цине.
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
Да, омул умблэ ка о умбрэ, се фрэмынтэ деӂяба, стрынӂе ла коморь ши ну штие чине ле ва луа.
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Акум, Доамне, че май пот нэдэждуи еу? Ын Тине ымь есте нэдеждя.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
Избэвеште-мэ де тоате фэрэделеӂиле меле! Ну мэ фаче де окара челуй небун!
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
Стау мут, ну дескид гура, кэч Ту лукрезь.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
Абате-Ць ловитуриле де ла мине! Ымь есе суфлетул суб ловитуриле мыний Тале.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
Ту педепсешть пе ом ши-л ловешть пентру фэрэделеӂя луй; ый прэпэдешть, ка молия, че аре ел май скумп. Да, орьче ом есте доар о суфларе.
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
Аскултэ-мь ругэчуня, Доамне, ши плякэ-Ць урекя ла стригэтеле меле! Ну тэчя ын фаца лакримилор меле! Кэч сунт ун стрэин ынаинтя Та, ун прибяг, ка тоць пэринций мей.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”
Абате-Ць привиря де ла мине ши ласэ-мэ сэ рэсуфлу, пынэ ну мэ дук ши сэ ну май фиу!

< Masalimo 39 >