< Masalimo 39 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
Przewodnikowi chóru, Jedutunowi. Psalm Dawida. Powiedziałem: Będę strzegł moich dróg, abym nie zgrzeszył językiem; nałożę na usta wędzidło, dopóki niegodziwy [będzie] przede mną.
2 Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
Zaniemówiłem oniemiały, zamilkłem [nawet] w dobrej [sprawie], lecz moja boleść się wzmagała.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
Rozgorzało we mnie serce; gdy rozmyślałem, zapłonął ogień, a [wtedy] mój język tak przemówił:
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
PANIE, daj mi poznać mój kres i miarę moich dni, abym wiedział, jak jestem słaby.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
Oto wymierzyłeś moje dni na szerokość dłoni, a mój wiek jest niczym przed tobą; zaprawdę każdy człowiek, nawet najlepszy, jest całkowitą marnością. (Sela)
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
Doprawdy człowiek przemija jak cień; doprawdy na próżno się kłopocze; gromadzi, a nie wie, kto to zabierze.
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
A teraz czego mam oczekiwać, Panie? W tobie jest moja nadzieja.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
Uwolnij mnie od wszystkich moich występków, nie wystawiaj mnie na pośmiewisko głupca.
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
Zamilkłem i nie otworzyłem moich ust, bo ty [to] sprawiłeś.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
Oddal ode mnie twoje karanie, bo ginę od uderzeń twojej ręki.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
Gdy karą chłoszczesz człowieka za nieprawość, [to] jak mól niszczysz jego piękno; doprawdy marnością jest każdy człowiek. (Sela)
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
Wysłuchaj mojej modlitwy, PANIE, i nakłoń ucha na moje wołanie; nie bądź głuchy na moje łzy, bo jestem gościem u ciebie [i] przychodniem, jak wszyscy moi ojcowie.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”
Oszczędzaj mnie, abym się wzmacniał, zanim odejdę i już mnie nie będzie.

< Masalimo 39 >