< Masalimo 39 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
Til Sangmesteren; til Jeduthun; en Psalme af David.
2 Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
Jeg sagde: Jeg vil vare paa mine Veje, at jeg ikke skal synde med min Tunge; jeg vil vare paa min Mund, at den holdes lukket, da den ugudelige endnu er for mig.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
Jeg var stum i Tavshed, jeg tav, uden at det blev godt; og min Smerte blev oprørt.
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
Mit Hjerte blev hedt inden i mig, under min Betænkning optændtes en Ild; jeg talte med min Tunge.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
Herre! lad mig kende mit Endeligt og mine Dages Maal, hvilket det monne være; maatte jeg kende, hvor snart jeg skal bort.
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
Se, du har sat mine Dage som en Haandbred og mit Livs Tid er som intet for dig; hvert Menneske er kun idel Forfængelighed, hvor fast han end staar. (Sela)
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Mennesket vandrer kun som et Skyggebillede, de gøre sig kun Uro forgæves; han samler og kan ikke vide, hvo der skal sanke det hjem.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
Og nu, Herre! hvad har jeg biet efter? Min Forventning er til dig.
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
Fri mig fra alle mine Overtrædelser, sæt mig ikke til Spot for Daaren!
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
Jeg var stum, jeg vilde ikke oplade min Mund; thi du har gjort det.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
Borttag din Plage fra mig; jeg er forgaaet ved din Haands Slag.
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
Tugter du nogen med megen Straf for Misgerning, da bringer du hans Herlighed til at hensmuldre ligesom Møl; alle Mennesker ere kun Forfængelighed. (Sela)
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”
Herre! hør min Bøn og vend dine Øren til mit Raab, ti ikke til min Graad; thi jeg er en fremmed hos dig, en Gæst som alle mine Fædre. Se bort fra mig, at jeg maa vederkvæges, førend jeg farer bort, og er ikke mere til.