< Masalimo 38 >
1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Dawid dwom. Adesrɛ. Awurade, nka mʼanim wɔ wʼabufuw mu na ntwe mʼaso wɔ wʼabufuwhyew mu.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Wo bɛmma hwirew me mu, na wo nsa adwerɛw me.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Wʼabufuwhyew no nti ahoɔden biara nni me mu; me bɔne nti, me nnompe ahodwow.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Mʼafɔdi amene me te sɛ adesoa a mu yɛ duru dodo.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Mʼakuru bɔn na aporɔw esiane me bɔne mu agyimisɛm nti.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Makotow na wɔabrɛ me ase; da mu nyinaa menantenantew twa agyaadwo.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Mʼakyi dompe mu yaw boro so: ahoɔden biara nni me nipadua mu.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Mabrɛ na mapɛtɛw koraa. Me koma mu yaw ma misi apini.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Awurade, nea merehwɛ anim nyinaa da wʼanim; mʼapinisi nhintaw wo.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Me koma bɔ kitirikitiri, na mʼahoɔden asa mpo mʼaniwa aduru sum.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Mʼapirakuru nti me nnamfonom ne me yɔnkonom mmɛn me; mʼafipamfo twe wɔn ho fi me ho.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Wɔn a wɔpɛ sɛ wokum me no sum me mfiri, wɔn a wɔpɛ sɛ wɔhaw me no di me sɛe ho nkɔmmɔ da mu nyinaa wodwen nnaadaasɛm ho.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Mete sɛ ɔsotifo a ɔnte asɛm, mete sɛ mum a ontumi nkasa.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Mayɛ sɛ obi a ɔnte asɛm, nea nʼano ntumi mma mmuae.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
Awurade, meretwɛn wo; Awurade me Nyankopɔn, wubegye me so.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Mekae se, “Mma wɔn ani nnye; anaa wɔmma wɔn ho so bere a mʼanan awatiri no.”
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Mereyɛ mahwe ase, na me yaw da so wɔ me mu.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Meka me mfomso kyerɛ; me bɔne hyɛ me so.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Bebree na wɔyɛ mʼatamfo; wɔn a wɔtan me kwa no dɔɔso.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Wɔn a wɔde bɔne tua me papa so ka no, bɔ me ahohora bere a mereyɛ papa.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Awurade nnyaw me. Me Nyankopɔn, nkɔ akyiri!
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Bra ntɛm bɛboa me, Awurade, mʼAgyenkwa. Wɔde ma dwonkyerɛfo no. Yedutun.