< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Yahwe, usinikemee katika hasira yako; usiniadhibu katika ghadhabu yako.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Kwa kuwa mishale yako hunichoma, na mkono wako huniangusha chini.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Mwili wangu wote unaumwa kwa sababu ya hasira yako; kwa sababu ya dhambi zangu mifupa yangu haina afya.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Kwa maana maovu yangu yamenielemea; yamekuwa mzigo mzito kwangu.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Vidonda vyangu vimeoza na vinanuka kwa sababu ya upumbavu wa dhambi zangu.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Nimepindika na kuwa mnyonge kila siku; ninaenenda katika maombolezo siku zote.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Kwa maana ndani yangu, ninaungua; hakuna afya katika mwili wangu.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Nimedhohofika na kulemewa sana; ninaugua kwa sababu ya dhiki yangu.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Bwana, wewe unaielewa shauku ya ndani kabisa ya moyo wangu, na kuugua kwangu hakujifichika kwako.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Moyo wangu unapwita pwita, nguvu zangu zinaniisha, macho yangu yanafifia.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Marafiki na ndugu zangu wamenitenga kwa sababu ya hali; majirani zangu hukaa mbali nami.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Wale wanaoutafuta uhai wangu hutega mitego kwa ajili yangu. Wao ambao hutafuta kunidhuru huongea maneno ya uharibifu na husema maneno ya uongo siku nzima.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Lakini, niko kama mtu kiziwi na sisikii lolote; niko kama mtu bubu ambaye hasemi lolote.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Niko kama mtu asiye sikia na mbaye hawezi kujibu.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
Hakika ninakungoja wewe, Yahwe; wewe utanijibu, Bwana Mungu wangu.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Ninasema hivi ili kwamba maadui zangu wasije wakafurahia juu yangu. Ikiwa mguu wangu utateleza, watanifanyia mambo mabaya.
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Kwa kuwa niko karibu mashakani, na niko katika maumivu ya mara kwa mara.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Ninatubu makosa yangu; ninahuzunika kwa dhambi zangu.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Lakini maadui zangu ni wengi; wale wanichukiao ni wengi.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Wao wananilipa mabaya kwa mema; wanavurumiza shutuma kwangu ingawa nimefuata lililo jema.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Usinitelekeze, Yahwe, Mungu wangu, usikae mbali nami.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Njoo haraka unisaidie, Bwana, wokovu wangu.

< Masalimo 38 >