< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Un Salmo de David, pidiendo a Dios que se acuerde de él. ¡Señor, por favor no me condenes, por causa de tu enojo conmigo! ¡No me castigues con tu furia!
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Tus flechas me han atravesado, tus manos han caído sobre mí.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Por tu enojo hacia mí, ni una sola parte de mi cuerpo está sana. Estoy completamente enfermo por mis pecados.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Me estoy ahogando en culpa. La carga es muy pesada de llevar.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Mis heridas están infectadas, están comenzando a oler mal, y por culpa de mi terquedad.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Estoy encorvado, retorcido por el dolor. Camino el día entero llorando y lamentándome.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Estoy ardiendo por dentro de fiebre. Ninguna parte de mi cuerpo está sana.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Estoy muy cansado, totalmente deshecho. Siento mi corazón como ruge de angustia.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Señor, sabes lo que quiero desesperadamente, escuchas cada respiración que tomo.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Mi corazón se está acelerando, dejándome sin fuerza. Mi vista está decayendo.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Mis amados y amigos no se me acercan porque tienen miedo de contagiarse. Incluso mi familia se ha distanciado.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Aquellos que intentan matarme me ponen trampas. Los que intentan herirme me amenazan, trabajando en sus planes engañosos todo el día.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Yo actúo como si fuera sordo con sus palabras, e intento parecer tonto para no tener que hablar.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Como un hombre que no puede oír, y que no responde, ¡Ese soy yo!
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
¡Porque espero en ti, Señor! Tú me responderás, Dios mío.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Señor, te pido que por favor mis enemigos no se jacten en frente mí, no dejes que se alegren cuando yo tropiece.
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Porque estoy por colapsar, el dolor nunca se detiene.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Confieso mis pecados. Lamento horriblemente todo lo que he hecho.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Tengo enemigos muy poderosos, son bastante activos, y me odian sin razón.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Me pagan el bien con mal. Me acusan por el bien que he tratado de hacer.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Señor, no me abandones, no te alejes de mí.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Apresúrate, ven y ayúdame, ¡Oh, Señor, mi salvador!

< Masalimo 38 >