< Masalimo 38 >
1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Dāvida dziesma, par piemiņu. Kungs, nesodi mani Savā dusmībā, un nepārmāci mani Savā bardzībā.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Jo Tavas bultas man ir iespiedušās, un Tava roka pār mani nolaidusies.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Nekādas veselības nav pie manas miesas caur Tavu dusmību, nekāda miera nav manos kaulos caur maniem grēkiem.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Jo mani noziegumi iet pāri pār manu galvu, kā grūta nasta tie man palikuši par daudz grūti.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Manas vātis smird un tek manas ģeķības dēļ.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Es eju salīcis un ļoti nospiests, cauru dienu es eju noskumis.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Jo manas iekšas ir moku pilnas, nekādas veselības nav pie manas miesas.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Es esmu pavisam sastindzis un sasists, es kaucu savas sirds vaimanās.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Kungs, Tavā priekšā ir visa mana kārošana, un mana nopūšanās Tev nav apslēpta.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Mana sirds trīc, mans spēks mani atstājis, arī pat manu acu gaismiņas man vairs nav.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Mani mīļie un mani draugi stāv tālu nost no manas mocības, un mani tuvākie stāv no tālienes.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Un kas manu dvēseli meklē, liek man valgus, un kas manu nelaimi meklē, runā postu un izdomā viltību cauru dienu.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Bet es esmu kā kurls, kas nedzird, un kā mēms, kas neatver savu muti.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Un es esmu kā vīrs, kas nedzird, un kam mutē vārdu pretim nav.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
Jo es gaidu, Kungs, uz Tevi, Tu paklausīsi, Kungs, mans Dievs.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Jo es sacīju: lai tie par mani nepriecājās; kad mana kāja šaubās, tad tie lai nelielās pret mani.
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Jo es esmu pie pašas krišanas un manas sāpes ir vienmēr manā priekšā.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Jo savu noziegumu es izsūdzu, un man ir bail manu grēku dēļ.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Bet mani ienaidnieki dzīvo un ir vareni, un kas mani par nepatiesu ienīst, tie vairojās.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Un kas ļaunu par labu maksā, tie stāv man pretim, tāpēc ka es uz labu dzenos.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Neatstājies no manis, Kungs, mans Dievs! neesi tālu no manis nost,
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Steidzies man palīgā, Kungs, mana pestīšana!