< Masalimo 38 >
1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Salmo. Di Davide. In memoria. Signore, non castigarmi nel tuo sdegno, non punirmi nella tua ira.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Le tue frecce mi hanno trafitto, su di me è scesa la tua mano.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Per il tuo sdegno non c'è in me nulla di sano, nulla è intatto nelle mie ossa per i miei peccati.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Le mie iniquità hanno superato il mio capo, come carico pesante mi hanno oppresso.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Putride e fetide sono le mie piaghe a causa della mia stoltezza.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Sono curvo e accasciato, triste mi aggiro tutto il giorno.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Sono torturati i miei fianchi, in me non c'è nulla di sano.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Afflitto e sfinito all'estremo, ruggisco per il fremito del mio cuore.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Signore, davanti a te ogni mio desiderio e il mio gemito a te non è nascosto.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Palpita il mio cuore, la forza mi abbandona, si spegne la luce dei miei occhi.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Amici e compagni si scostano dalle mie piaghe, i miei vicini stanno a distanza.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Tende lacci chi attenta alla mia vita, trama insidie chi cerca la mia rovina. e tutto il giorno medita inganni.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Io, come un sordo, non ascolto e come un muto non apro la bocca;
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
sono come un uomo che non sente e non risponde.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
In te spero, Signore; tu mi risponderai, Signore Dio mio.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Ho detto: «Di me non godano, contro di me non si vantino quando il mio piede vacilla».
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Poiché io sto per cadere e ho sempre dinanzi la mia pena.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Ecco, confesso la mia colpa, sono in ansia per il mio peccato.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
I miei nemici sono vivi e forti, troppi mi odiano senza motivo,
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
mi pagano il bene col male, mi accusano perché cerco il bene.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Non abbandonarmi, Signore, Dio mio, da me non stare lontano;
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
accorri in mio aiuto, Signore, mia salvezza.