< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Psaume de David, en souvenir touchant le sabbat. Seigneur, ne me reprenez pas dans votre fureur, et dans votre colère ne me châtiez pas.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Parce que j’ai été percé de vos flèches; et que vous avez appesanti sur moi votre main.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Il n’y a rien de sain dans ma chair en présence de votre fureur: il n’y a pas de paix dans mes os en présence de mes péchés.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Parce que mes iniquités se sont élevées au-dessus de ma tête; et comme un fardeau pesant, elles se sont appesanties sur moi.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Mes plaies se sont putréfiées et corrompues en présence de ma folie.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Je suis devenu malheureux, et je suis entièrement courbé: et tout le jour je marchais contristé.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Parce que mes reins ont été remplis d’illusions, et qu’il n’y a rien de sain dans ma chair.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
J’ai été affligé et j’ai été humilié à l’excès; je rugissais dans le frémissement de mon cœur.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Seigneur, devant vous est tout mon désir, mon gémissement ne vous est pas caché.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Mon cœur a été troublé, ma force m’a abandonné, et la lumière de mes yeux, elle-même n’est plus avec moi.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Mes amis et mes proches se sont approchés vis-à-vis de moi, et ils se sont arrêtés. Et ceux qui étaient près de moi s’en sont tenus éloignés:
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Et ceux qui cherchaient mon âme usaient de violence envers moi.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Mais moi, comme un sourd, je n’entendais pas; et j’étais comme un muet qui n’ouvre pas la bouche.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Je suis donc devenu comme un homme qui n’entend point, et qui n’a pas dans sa bouche de répliques.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
Parce que c’est vous. Seigneur, en qui j’ai espéré: c’est vous qui m’exaucerez. Seigneur mon Dieu.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Parce que j’ai dit: Que mes ennemis ne se réjouissent jamais à mon sujet: et tandis que mes pieds étaient chancelants, ils ont parlé à mon sujet avec orgueil.
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Parce que moi je suis prêt à des châtiments, et que ma douleur est toujours en ma présence.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Parce que je publierai mon iniquité; et que je penserai à mon péché.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Mais mes ennemis vivent et se sont fortifiés contre moi; et ils se sont multipliés ceux qui me haïssent injustement.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Ceux qui me rendent des maux pour des biens me déchiraient, parce que je m’attachais au bien.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Ne m’abandonnez pas, Seigneur mon Dieu; ne vous éloignez pas de moi.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Songez à me secourir, Seigneur, Dieu de mon salut.

< Masalimo 38 >