< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Psaume de David. Pour la Commémoration. Eternel, ne me réprimande pas dans ton irritation, ne me châtie pas dans ton courroux.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Car tes flèches m’ont transpercé, et ta main s’est appesantie sur moi.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Ta colère n’a laissé rien d’intact dans mon corps, mes péchés ont banni la paix de mes membres.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Car mes fautes ont monté par-dessus ma tête; comme un gros poids, elles pèsent lourdement sur moi.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Mes plaies sont fétides, putréfiées, par suite de mon égarement.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Je suis tordu, affaissé outre mesure; tout le temps, je marche voilé de tristesse,
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
car mes entrailles sont toutes malades d’inflammation; nulle partie saine en mon corps.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Je suis épuisé, abattu au dernier point, je pousse des cris dans la violente agitation de mon cœur.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Seigneur, tout ce que je souhaite t’est connu; mes soupirs ne t’échappent point.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Mon cœur palpite violemment, ma vigueur m’a abandonné, même la lumière de mes yeux me fait défaut.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Mes amis, mes compagnons se tiennent à l’écart de mon mal, mes proches demeurent à distance.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Ceux qui en veulent à ma vie me dressent des embûches, ceux qui cherchent mon malheur disent des paroles meurtrières, méditent des perfidies toute la journée.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Pourtant, moi, tel un sourd, je n’entends point, je suis comme un muet qui n’ouvre pas la bouche.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Oui, je me comporte comme un homme qui n’entend pas, et qui n’a pas de répliques sur les lèvres.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
C’Est que je tourne mon attente vers toi; et, toi, tu m’exauceras, Seigneur, mon Dieu.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
C’Est que je me dis: "Ils pourraient se réjouir de moi, faire les fiers à mon endroit, en voyant chanceler mes pas!"
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Ne suis-je point désigné à la ruine? Mon mal n’est-il pas toujours là, sous mes yeux?
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Car il faut que je confesse mon iniquité; je suis alarmé de mon péché,
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
alors que mes ennemis ont une grande puissance de vie; nombreux sont ceux qui me haïssent sans cause,
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
et qui, rendant le mal pour le bien, me molestent pour me récompenser de poursuivre le bien.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Ne me délaisse pas, ô Eternel! Mon Dieu, ne te tiens pas éloigné de moi.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Hâte-toi de me secourir, Seigneur, qui es mon protecteur.

< Masalimo 38 >