< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Yahweh, when you are angry [with me], do not rebuke/scold me and punish me!
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
[Now it is as though] you have shot your arrows at me and wounded me; you have struck me and knocked me down.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Because you have been angry with me, I am suffering great pain. Because of my sin, my whole body is diseased.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
All my sins are [like a flood] that covers my head; they are like a load that is very heavy, with the result that I cannot carry it.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Because I have done foolish things, I have sores that have become worse, and they stink.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
[Sometimes] I am bent over, and [sometimes] I lie prostrate; I am sad/cry all day.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
My body is burning with fever, and I am very ill.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
I am completely exhausted, and I have no strength. I am very distressed, and I groan with pain.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Yahweh, you know that I desire [to be healed]; you hear me while I am groaning.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
My heat is pounding heavily, and all my strength is gone. I am no longer able to see well.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
My friends and neighbors stay away from me because of my sores; even my own family stays away from me.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
And those who want to kill me set traps to catch me; those who want to harm me discuss ways to get rid of me; they plot against me all day.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Now I act like I’m deaf, and do not listen [to what they say]. I act like I cannot talk, so I say nothing [to reply to them].
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
I act like a man who does not answer [when people talk to him], because he cannot hear anything.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
But Yahweh, I trust in you. My Lord God, you will answer me.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
I said to you, “Do not cause [me to die, with the result that] my enemies will rejoice! Do not cause me to stumble, with the result that they will be very happy!”
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
I say that because I am about to fall down, and I constantly have pain.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
I confess the wrong things that I have done; I am [very] sorry for the sins that I have committed.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
My enemies are healthy and strong; there are many people who hate me for no reason.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Those who do evil things to me in return for my doing good things to them oppose me because I try to do what is right.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Yahweh, do not abandon me! My God, do not stay far from me!
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Lord, you are the one who saves/rescues me; Quickly [come and] help me!

< Masalimo 38 >