< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Žalm Davidův k připomínání. Hospodine, v prchlivosti své netresci mne, ani v hněvě svém kárej mne.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Nebo střely tvé uvázly ve mně, a ruka tvá na mne těžce dolehla.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
Nic není celého v těle mém pro tvou hněvivost, nemají pokoje kosti mé pro hřích můj.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Nebo nepravosti mé vzešly nad hlavu mou, jako břímě těžké nemožné jsou mi k unesení.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Zahnojily se, a kyší rány mé pro bláznovství mé.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Pohrbený a sklíčený jsem náramně, každého dne v smutku chodím.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Nebo ledví má plná jsou mrzkosti, a nic není celého v těle mém.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Zemdlen jsem a potřín převelice, řvu pro úzkost srdce svého.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Pane, před tebou jest všecka žádost má, a vzdychání mé není před tebou skryto.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Srdce mé zmítá se, opustila mne síla má, i to světlo očí mých není se mnou.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Ti, kteříž mne milovali, a tovaryši moji, štítí se ran mých, a příbuzní moji zdaleka stojí.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Ti pak, kteříž stojí o bezživotí mé, osídla lécejí, a kteříž mého zlého hledají, mluví převráceně, a přes celý den lest a chytrost smýšlejí.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Ale já jako hluchý neslyším, a jako němý, kterýž neotvírá úst svých;
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Tak jsem, jako člověk, kterýž neslyší, a v jehož ústech není žádného odporu.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
Nebo na tě, Hospodine, očekávám, ty za mne odpovíš, Pane Bože můj.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Nebo jsem řekl: Ať se neradují ze mne, poklesla-li by se noha má, ať se pyšně nepozdvihují nade mnou,
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Poněvadž k snášení bíd hotov jsem, anobrž bolest má vždycky jest přede mnou.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
A že nepravosti své vyznávám, a pro hřích svůj tesklím.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Pročež nepřátelé moji veseli jsouce, silí se, a rozmnožují se ti, kteříž mne bez příčiny nenávidí.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
A zlým za dobré mi se odplacujíce, činí mi protivenství, proto že dobrého následuji.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Neopouštějž mne, Hospodine Bože můj, nevzdalujž se ode mne.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Přispěj k spomožení mému, Pane spasení mého.

< Masalimo 38 >