< Masalimo 37 >

1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
Pesem Davidova. Ne razsrdi se zaradi hudobnih, ne zavidaj njih, ki delajo krivico.
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
Ker hitro se pokosé kakor seno, in kakor nežne trave zelenje odpadejo.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Zaupaj v Gospoda in delaj dobro; prebivaj v deželi in v poštenosti se pasi.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
In razveseljuj se v Gospodu, ki ti bode dal srca tvojega prošnje.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Izróči Gospodu svojo pot in zaupaj vanj; on bode že storil.
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
Kakor luč bode pokazal pravičnost tvojo, in pravico tvojo kakor poldan.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Zanašaj se na Gospoda in čakaj ga neprestano: ne razsrdi se zaradi njega, ki ima srečo na poti svoji; zaradi moža, ki doprinaša, kar misli.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Odjenjaj od jeze, in pústí togoto, ne razsrdi se, da bi le hudo storil.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
Ker hudobniki se bodejo iztrebili: čakajoči pa Gospoda dedovali bodejo sami deželo.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
In še malo, in celo ne bode krivičnega: ko bodeš ogledoval mesto njegovo, ne bode ga.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
Krotki pa bodejo dedovali deželo, in radovali se bodejo v obilosti mirú.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
Ko misli krivični zoper pravičnega, in škriplje sè zobmí svojimi proti njemu,
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
Smeje se mu Gospod, ker vidi, da prihaja dan njegov.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
Meč naj so potegnili krivični in lok svoj napéli, da poderó ubozega in siromaka, da pobijejo poštene na potu:
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
Meč njihov predere njih srce, in zdrobé se njihovi loki.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Dobro je vsakemu pravičnemu malo, bolje nego obilost mnogim krivičnim.
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
Ker roke krivičnih se zdrobé, pravične pa podpira Gospod.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
Gospod pozna čase poštenih, tako da bode posest njihova vekomaj.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
Osramoté se ne o hudem času; temuč nasitijo se o lakoti času,
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
Ko krivični poginejo in sovražniki Gospoda kakor kar je drazega v jagnjetih, kakor to mine v dim, minejo oni.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
Na pósodo jemlje krivični, a vrniti ne more; pravični pa je milosten in daruje:
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Ker blagoslovljeni po njem podedovajo deželo, prokleti pa po njem pogubé se.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
Gospod stavi stopinje možu, katerega poti se raduje.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
Ko pada, ne zvrne se; ker Gospod podpira roko njegovo.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
Otrok sem bil, postaral sem se tudi, ali videl nisem pravičnege zapuščenega tako, da bi kruha iskalo seme njegovo.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
Ves dan deli milost in posoja, in v blagoslovu je seme njegovo.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Odstopi od hudega, in delaj dobro; tako prebivaj vekomaj.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
Ker Gospod ljubi pravico, in ne zapusti njih, katerim je dobrovoljen; na veke se ohrani, seme pa krivičnih se iztrebi.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
Pravični bodo podedovali deželo, in prebivali bodo večno v njej.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
Pravičnega usta premišljajo modrost, in jezik njegov govori pravico.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
V srci njegovem je postava njegovega Boga, noga njegova ne omahuje na hojah svojih.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
Krivični pa zalezuje pravičnega in želi ga umoriti.
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
Gospod ga ne zapusti v roki njegovi, ne dovoli, da se obsodi, ko se sodi.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Pazi na Gospoda in drži se poti njegove: tedaj te povzdigne, da bodeš podedoval deželo, videl krivičnih pogubo.
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
Videl sem krivičnega, ko je pognal z veliko močjo, in se razvijal kakor domače drevo zeleneče.
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
Potem je minil, in glej, ni ga bilo več: ker iskal sem ga, a našel se ni.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Opazuj poštenega, in glej pravičnega, konec tega moža je mir.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
Grešniki pa se pogubljajo vsi vkup; konec krivičnih se iztrebi.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
Ker blaginja njih je od Gospoda, moč njih o času stiske.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
In pomaga jim Gospod ter otima jih; otima jih krivičnih ter jih ohranja, ker pribegajo k njemu.

< Masalimo 37 >