< Masalimo 37 >

1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
Zabbuli ya Dawudi. Teweeraliikiriranga olw’abantu ababi, so tokwatirwanga buggya abo abakola ebitasaana.
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
Kubanga bagenda kuwotoka ng’omuddo, bafiire ddala ng’essubi ekkalu.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Weesigenga Mukama okolenga bulungi, onoobeeranga n’emirembe mu nsi n’ofuna ebirungi.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
Sanyukiranga mu Mukama, anaakuwanga omutima gwo bye gwetaaga.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
By’okola byonna byesigamyenga ku Mukama; mwesigenga, anaakukoleranga ky’oyagala.
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
Anaayolekanga obutuukirivu bwo ng’omusana, n’obwenkanya bw’ebikolwa byo ne bwakaayakana ng’enjuba ey’omu ttuntu.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Siriikirira awali Mukama, ogumiikirize ng’olindirira ky’anaakola. Tofangayo ng’abalala bafunye ebirungi nga bayita mu kutetenkanya kwabwe okubi.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Tonyiiganga era weewale ekiruyi; teweeraliikiriranga kubanga bivaamu bibi byereere.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
Kubanga ababi balisalibwako, naye abeesiga Mukama baligabana ensi.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
Wanaayitawo akabanga katono ababi baggweerewo ddala; wadde mulibanoonya temulibalabako.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
Naye abateefu baligabana ensi ne beeyagalira mu ddembe eritatendeka.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
Ababi basalira abatuukirivu enkwe, ne babalumira obujiji.
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
Naye Mukama asekerera ababi, kubanga amanyi ng’entuuko zaabwe ziri kumpi.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
Ababi basowoddeyo ebitala byabwe ne baleega emitego gy’obusaale, batte abaavu n’abali mu kwetaaga era basaanyeewo abo abatambulira mu kkubo eggolokofu.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
Naye ebitala byabwe birifumita mitima gyabwe gyennyini, n’emitego gyabwe egy’obusaale girimenyebwa.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Ebitono omutuukirivu by’alina bisinga obugagga bw’ababi abangi;
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
kubanga amaanyi g’abakola ebibi galikoma, naye Mukama anaawaniriranga abatuukirivu.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
Ennaku z’abataliiko kya kunenyezebwa, zimanyibwa Mukama, era omugabo gwabwe gunaabanga gwa lubeerera.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
Mu biseera eby’akabi ebyakatyabaga tebaayongoberenga, ne mu biro eby’enjala banakkusibwanga.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
Naye ababi balizikirira; abalabe ba Mukama balifaanana ng’obulungi bwe ttale, era baliggwaawo, baliggwaawo ng’omukka.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
Ababi beewola, ne batasasula; naye abatuukirivu basaasira era bagaba bingi.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Abo Mukama b’awa omukisa baligabana ensi, naye abo b’akolimira balizikirizibwa.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
Mukama bw’asanyukira ekkubo ly’omuntu, aluŋŋamya entambula ye.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
Ne bw’aneesittalanga, taagwenga wansi, kubanga omukono gwa Mukama gumuwanirira.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
Nnali muto kati nkaddiye, naye sirabanga batuukirivu nga balekeddwa ttayo, wadde abaana baabwe nga basabiriza ekyokulya.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
Bagaba bingi bulijjo, era baazika ku byabwe n’essanyu. Abaana baabwe banaaweebwanga omukisa.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Muve mu bibi, mukolenga ebirungi, munaabanga balamu emirembe gyonna.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
Kubanga Mukama ayagala ab’amazima, n’abeesigwa be taabaabulirenga. Banaalabirirwanga emirembe gyonna; naye ezzadde ly’ababi lirizikirizibwa.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
Abatuukirivu baligabana ensi ne babeeranga omwo emirembe gyonna.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
Akamwa k’omutuukirivu koogera bya magezi, n’olulimi lwe lwogera bya mazima.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
Amateeka ga Katonda we gali mu mutima gwe, era ebigere bye tebiseerera.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
Omubi ateega omutuukirivu ng’anoonya okumutta,
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
naye Mukama taliganya babi kuwangula, wadde okukkiriza abatuukirivu okusingibwa omusango.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Lindirira Mukama n’okugumiikiriza, otambulirenga mu makubo ge; naye alikugulumiza n’akuwa ensi; ababi bwe balisalirwako olikitegeera.
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
Nalaba omuntu omubi era omukambwe ennyo, naye nga buli ky’akola kimugendera bulungi, ng’agimuse ng’omuti ogukulidde mu ttaka eggimu,
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
naye teyalwawo n’abula, ne mmumagamaga buli wantu, nga talabikako.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Tunuulira omuntu ataliiko kya kunenyezebwa, wekkaanye oyo omulongoofu; obulamu bwe bunajjulanga emirembe.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
Naye aboonoonyi bonna balizikirizibwa; ezzadde ly’ababi lirisaanyizibwawo.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
Obulokozi bw’abatuukirivu buva eri Mukama; ye ky’ekigo kyabwe ekinywevu gye baddukira mu kiseera eky’emitawaana.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
Mukama abayamba n’abalokola; abaggya mu mikono gy’ababi n’abalokola, kubanga gy’ali gye baddukira.

< Masalimo 37 >