< Masalimo 37 >
1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
(다윗의 시) 행악자를 인하여 불평하여 하지 말며 불의를 행하는 자를 투기하지 말지어다
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
저희는 풀과 같이 속히 베임을 볼 것이며 푸른 채소 같이 쇠잔할 것임이로다
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
여호와를 의뢰하여 선을 행하라! 땅에 거하여 그의 성실로 식물을 삼을지어다
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
또 여호와를 기뻐하라! 저가 네 마음의 소원을 이루어 주시리로다
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
너의 길을 여호와께 맡기라! 저를 의지하면 저가 이루시고
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
네 의를 빛같이 나타내시며 네 공의를 정오의 빛같이 하시리로다
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
여호와 앞에 잠잠하고 참아 기다리라! 자기 길이 형통하며 악한 꾀를 이루는 자를 인하여 불평하여 말지어다
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
분을 그치고 노를 버리라 불평하여 말라 행악에 치우칠 뿐이라
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
대저 행악하는 자는 끊어질 것이나 여호와를 기대하는 자는 땅을 차지하리로다
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
잠시 후에 악인이 없어지리니 네가 그곳을 자세히 살필지라도 없으리로다
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
오직 온유한 자는 땅을 차지하며 풍부한 화평으로 즐기리로다
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
악인이 의인 치기를 꾀하고 향하여 그 이를 가는도다
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
주께서 저를 웃으시리니 그 날의 이름을 보심이로다
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
악인이 칼을 빼고 활을 당기어 가난하고 궁핍한 자를 엎드러뜨리며 행위가 정직한 자를 죽이고자 하나
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
그 칼은 자기의 마음을 찌르고 그 활은 부러지리로다
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
의인의 적은 소유가 많은 악인의 풍부함보다 승하도다
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
악인의 팔은 부러지나 의인은 여호와께서 붙드시는도다
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
여호와께서 완전한 자의 날을 아시니 저희 기업은 영원하리로다
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
저희는 환난 때에 부끄럽지 아니하며 기근의 날에도 풍족하려니와
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
악인은 멸망하고 여호와의 원수는 어린 양의 기름 같이 타서 연기되어 없어지리로다
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
악인은 꾸고 갚지 아니하나 의인은 은혜를 베풀고 주는도다
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
주의 복을 받은 자는 땅을 차지하고 주의 저주를 받은 자는 끊어지리로다
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
여호와께서 사람의 걸음을 정하시고 그 길을 기뻐하시나니
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
저는 넘어지나 아주 엎드러지지 아니함은 여호와께서 손으로 붙드심이로다
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
내가 어려서부터 늙기까지 의인이 버림을 당하거나 그 자손이 걸식함을 보지 못하였도다
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
저는 종일토록 은혜를 베풀고 꾸어 주니 그 자손이 복을 받는도다
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
악에서 떠나 선을 행하라! 그리하면 영영히 거하리니
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
여호와께서 공의를 사랑하시고 그 성도를 버리지 아니하심이로다 저희는 영영히 보호를 받으나 악인의 자손은 끊어지리로다
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
의인이 땅을 차지함이여 거기 영영히 거하리로다
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
의인의 입은 지혜를 말하고 그 혀는 공의를 이르며
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
그 마음에는 하나님의 법이 있으니 그 걸음에 실족함이 없으리로다
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
악인이 의인을 엿보아 살해할 기회를 찾으나
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
여호와는 저를 그 손에 버려두지 아니하시고 재판 때에도 정죄치 아니하시리로다
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
여호와를 바라고 그 도를 지키라! 그리하면 너를 들어 땅을 차지하게 하실 것이라 악인이 끊어질 때에 네가 목도하리로다
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
내가 악인의 큰 세력을 본즉 그 본토에 선 푸른 나무의 무성함 같으나
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
사람이 지날 때에 저가 없어졌으니 내가 찾아도 발견치 못하였도다
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
완전한 사람을 살피고 정직한 자를 볼지어다 화평한 자의 결국은 평안이로다
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
범죄자들은 함께 멸망하리니 악인의 결국은 끊어질 것이나
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
의인의 구원은 여호와께 있으니 그는 환난 때에 저희 산성이시로다
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
여호와께서 저희를 도와 건지시되 악인에게서 건져 구원하심은 그를 의지한 연고로다