< Masalimo 37 >

1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
Di Davide. Non ti crucciare a cagion de’ malvagi; non portare invidia a quelli che operano perversamente;
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
perché saran di subito falciati come il fieno, e appassiranno come l’erba verde.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Confidati nell’Eterno e fa’ il bene; abita il paese e coltiva la fedeltà.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
Prendi il tuo diletto nell’Eterno, ed egli ti darà quel che il tuo cuore domanda.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Rimetti la tua sorte nell’Eterno; confidati in lui, ed egli opererà
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
Egli farà risplendere la tua giustizia come la luce, e il tuo diritto come il mezzodì.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Sta’ in silenzio dinanzi all’Eterno, e aspettalo; non ti crucciare per colui che prospera nella sua via, per l’uomo che riesce ne’ suoi malvagi disegni.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Cessa dall’ira e lascia lo sdegno; non crucciarti; ciò non conduce che al mal fare.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
Poiché i malvagi saranno sterminati; ma quelli che sperano nell’Eterno possederanno la terra.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
Ancora un poco e l’empio non sarà più; tu osserverai il suo luogo, ed egli non vi sarà più.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
Ma i mansueti erederanno la terra e godranno abbondanza di pace.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
L’empio macchina contro il giusto e digrigna i denti contro lui.
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
Il Signore si ride di lui, perché vede che il suo giorno viene.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
Gli empi han tratto la spada e teso il loro arco per abbattere il misero e il bisognoso, per sgozzare quelli che vanno per la via diritta.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
La loro spada entrerà loro nel cuore, e gli archi loro saranno rotti.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Meglio vale il poco del giusto che l’abbondanza di molti empi.
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
Perché le braccia degli empi saranno rotte; ma l’Eterno sostiene i giusti.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
L’Eterno conosce i giorni degli uomini integri; e la loro eredità durerà in perpetuo.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
Essi non saran confusi nel tempo dell’avversità, e saranno saziati nel tempo dalla fame.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
Ma gli empi periranno; e i nemici dell’Eterno, come grasso d’agnelli, saran consumati e andranno in fumo.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
L’empio prende a prestito e non rende; ma il giusto è pietoso e dona.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Poiché quelli che Dio benedice erederanno la terra, ma quelli ch’ei maledice saranno sterminati.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
I passi dell’uomo dabbene son diretti dall’Eterno ed egli gradisce le vie di lui.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
Se cade, non è però atterrato, perché l’Eterno lo sostiene per la mano.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
Io sono stato giovane e son anche divenuto vecchio, ma non ho visto il giusto abbandonato, né la sua progenie accattare il pane.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
Egli tutti i giorni è pietoso e presta, e la sua progenie è in benedizione.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Ritraiti dal male e fa’ il bene, e dimorerai nel paese in perpetuo.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
Poiché l’Eterno ama la giustizia e non abbandona i suoi santi; essi son conservati in perpetuo; ma la progenie degli empi sarà sterminata.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
I giusti erederanno la terra e l’abiteranno in perpetuo.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
La bocca del giusto proferisce sapienza e la sua lingua pronunzia giustizia.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
La legge del suo Dio è nel suo cuore; i suoi passi non vacilleranno.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
L’empio spia il giusto e cerca di farlo morire.
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
L’Eterno non l’abbandonerà nelle sue mani, e non lo condannerà quando verrà in giudicio.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Aspetta l’Eterno e osserva la sua via; egli t’innalzerà perché tu eredi la terra; e quando gli empi saranno sterminati, tu lo vedrai.
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
Io ho veduto l’empio potente, e distendersi come albero verde sul suolo natìo;
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
ma è passato via, ed ecco, non è più; io l’ho cercato, ma non s’è più trovato.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Osserva l’uomo integro e considera l’uomo retto; perché v’è una posterità per l’uomo di pace.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
Mentre i trasgressori saranno tutti quanti distrutti; la posterità degli empi sarà sterminata.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
Ma la salvezza dei giusti procede dall’Eterno; egli è la loro fortezza nel tempo della distretta.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
L’Eterno li aiuta e li libera: li libera dagli empi e li salva, perché si sono rifugiati in lui.

< Masalimo 37 >