< Masalimo 37 >

1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
[S. die Anm. zu Ps. 25] N [Von David.] Erzürne dich nicht über die Übeltäter, beneide nicht die, welche Unrecht tun!
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
Denn wie das Gras werden sie schnell vergehen, und wie das grüne Kraut verwelken. [Eig. hinwelken]
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Vertraue auf Jehova und tue Gutes; wohne im Lande und weide dich an Treue; [Eig. weide, od. pflege [übe] Treue]
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
und ergötze dich an Jehova: so wird er dir geben die Bitten deines Herzens.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Befiehl [W. Wälze auf] Jehova deinen Weg und vertraue auf ihn! und er wird handeln;
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
und er wird deine Gerechtigkeit hervorkommen lassen wie das Licht, und dein Recht wie den Mittag.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Vertraue still [W. Sei still] dem Jehova und harre auf ihn! Erzürne dich nicht über den, dessen Weg gelingt, über den Mann, der böse Anschläge ausführt!
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Stehe ab vom Zorn und laß den Grimm! Erzürne dich nicht! nur zum Übeltun verleitet es.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
Denn die Übeltäter werden ausgerottet werden; aber die auf Jehova hoffen, diese werden das Land besitzen.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
Und noch um ein Kleines, und der Gesetzlose ist nicht mehr; und siehst du dich um nach seiner Stätte, so ist er [O. sie] nicht da.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
Aber die Sanftmütigen werden das Land besitzen, und werden sich ergötzen an Fülle von Wohlfahrt.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
Der Gesetzlose sinnt wider den Gerechten, und mit seinen Zähnen knirscht er wider ihn.
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
Der Herr lacht seiner, denn er sieht, daß sein Tag kommt.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
Die Gesetzlosen haben das Schwert gezogen und ihren Bogen gespannt, um zu fällen den Elenden und den Armen, hinzuschlachten, die in Geradheit wandeln.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
Ihr Schwert wird in ihr eigenes Herz dringen, und ihre Bogen werden zerbrochen werden.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Besser das Wenige des Gerechten, als der Überfluß vieler Gesetzlosen.
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
Denn die Arme der Gesetzlosen werden zerbrochen werden, aber Jehova stützt die Gerechten.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
Jehova kennt [d. h. nimmt Kenntnis von] die Tage derer, die lauter [O. vollkommen, tadellos] sind, und ihr Erbteil wird ewig sein;
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
sie werden nicht beschämt werden in der Zeit des Übels, und in den Tagen des Hungers werden sie gesättigt werden.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
Denn die Gesetzlosen werden umkommen, und die Feinde Jehovas sind wie die Pracht der Auen; [And.: wie das Fett der Lämmer] sie schwinden, sie schwinden dahin wie Rauch.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
Der Gesetzlose borgt und erstattet nicht wieder; der Gerechte aber ist gnädig und gibt.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Denn die von ihm Gesegneten werden das Land besitzen, und die von ihm Verfluchten werden ausgerottet werden.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
Von Jehova werden befestigt des Mannes Schritte, und an seinem Wege hat er Wohlgefallen;
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
wenn er fällt, wird er nicht hingestreckt werden, denn Jehova stützt seine Hand.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
Ich war jung und bin auch alt geworden, und nie sah ich den Gerechten verlassen, noch seinen Samen nach Brot gehen;
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
den ganzen Tag ist er gnädig und leiht, und sein Same wird gesegnet sein. [W. ist für Segen]
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Weiche vom Bösen und tue Gutes, und bleibe [O. so wirst du bleiben [im Lande wohnen]] ewiglich!
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
Denn Jehova liebt das Recht und wird seine Frommen nicht verlassen; ewig werden sie bewahrt, aber der Same der Gesetzlosen wird ausgerottet.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
Die Gerechten werden das Land besitzen und werden darin wohnen immerdar.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
Der Mund des Gerechten spricht Weisheit aus, und seine Zunge redet das Recht;
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
das Gesetz seines Gottes ist in seinem Herzen, seine Schritte werden nicht wanken.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
Der Gesetzlose lauert auf den Gerechten und sucht ihn zu töten;
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
Jehova wird ihn nicht in seiner Hand lassen, und ihn nicht verdammen, wenn er gerichtet wird.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Harre auf Jehova und bewahre seinen Weg, und er wird dich erhöhen, das Land zu besitzen. Wenn die Gesetzlosen ausgerottet werden, wirst du zusehen. [O. An der Ausrottung der Gesetzlosen wirst du deine Lust sehen]
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
Ich habe einen Gesetzlosen gesehen, der gewaltig [Zugleich: gewalttätig] war, und der sich ausbreitete wie ein nicht verpflanzter grüner [O. saftvoller] Baum;
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
und man ging vorbei, und siehe, er war nicht mehr; und ich suchte ihn, und er ward nicht gefunden.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Achte auf den Unsträflichen und sieh auf den Aufrichtigen; denn für den Mann des Friedens gibt es eine Zukunft. [O. Nachkommenschaft; wie Ps. 109,13]
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
Die Übertreter aber werden vertilgt allesamt, es wird abgeschnitten die Zukunft [O. Nachkommenschaft; wie Psalm 109,13] der Gesetzlosen.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
Aber die Rettung der Gerechten ist von Jehova, der ihre Stärke [Eig. Feste, Schutzwehr] ist zur Zeit der Bedrängnis;
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
und Jehova wird ihnen helfen und sie erretten; er wird sie erretten von den Gesetzlosen und ihnen Rettung verschaffen, denn sie trauen auf ihn.

< Masalimo 37 >