< Masalimo 37 >
1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
De David. Ne cherche pas à imiter les méchants; ne porte pas envie à ceux qui font le mal.
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
Car, comme l'herbe des champs, ils seront bientôt flétris; comme la plante verte, ils ne tarderont pas à tomber.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Espère au Seigneur et fais le bien; habite la terre, et tu seras nourri de ses richesses.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
Délecte-toi dans le Seigneur, et il t'accordera ce que ton cœur aura demandé.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Révèle au Seigneur ta voie; espère en lui, et il agira.
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
Il manifestera ta justice comme une lumière, et ton jugement comme le midi.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Soumets-toi au Seigneur, et prie-le; ne porte pas envie à celui qui prospère dans sa voie, à l'homme qui commet des injustices.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Calme ta colère, laisse tomber ton courroux; ne cherche pas à devenir méchant;
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
Car les méchants seront exterminés; mais ceux qui attendent le Seigneur auront la terre pour héritage.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
Encore un peu de temps, et le pécheur ne sera plus; tu chercheras sa place, et tu ne la trouveras point.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
Mais les doux auront la terre pour héritage, et ils se délecteront dans la plénitude de la paix.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
Le pécheur épiera le juste, et il grincera des dents contre lui.
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
Et le Seigneur se rira de lui; car il voit que son jour approche.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
Les pécheurs ont tiré l'épée; ils ont tendu leur arc pour abattre le pauvre et l'indigent, pour tuer ceux qui ont le cœur droit.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
Que leur glaive s'enfonce dans leur propre cœur, et que leur arc soit brisé!
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Mieux vaut la pauvreté du juste que les grandes richesses des pécheurs;
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
Car les bras des pécheurs seront broyés, et le Seigneur affermit les justes.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
Le Seigneur connaît les voies des innocents, et leur héritage sera éternel.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
Dans les temps de détresse, ils ne seront point confondus, et aux jours de famine ils seront rassasiés.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
Mais les pécheurs périront, et les ennemis de Dieu sont à peine parvenus aux honneurs et à la gloire qu'ils s'évanouissent comme une fumée qui se disperse.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
Le pécheur emprunte, et il ne rendra pas; le juste a compassion, et il donne.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Ceux qui bénissent le Seigneur auront la terre pour héritage; ceux qui le maudissent seront exterminés.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
Les pas de l'homme sont conduits par le Seigneur, qui se complaira dans sa voie.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
S'il tombe, il ne se brisera point; car le Seigneur le soutient de sa main.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
J'ai été jeune et je suis devenu vieux, et je n'ai point vu le juste délaissé, ni ses enfants demander leur pain.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
Il est compatissant, et chaque jour il prête, et sa race sera bénie.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Détourne-toi du mal et fais le bien, et habite la terre dans les siècles des siècles.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
Car le Seigneur aime la justice, et il n'abandonnera jamais ses saints; il les prendra sous garde éternellement; les innocents seront vengés, et la race des impies sera détruite.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
Les justes auront la terre pour héritage, et ils l'habiteront durant les siècles des siècles.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
La bouche du juste méditera la sagesse, et sa langue parlera la justice.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
La loi de son Dieu est dans son cœur, et ses pas ne seront jamais chancelants.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
Le pécheur épie le juste; il cherche à le faire périr.
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
Mais le Seigneur ne le laissera pas en ses mains, et il ne le condamnera pas lorsqu'il sera jugé par le pécheur.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Attends le Seigneur et garde sa voie, et il t'élèvera pour que tu hérites de la terre; et lorsque les pécheurs auront péri, tu verras!
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
J'ai vu l'impie fier, exalté et élevé comme les cèdres du Liban:
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
J'ai passé et voilà qu'il n'était plus; et je l'ai cherché, et sa place n'a point été retrouvée.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Garde l'innocence, aie en vue la droiture; car il a une attente l'homme pacifique.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
Mais les pervers seront exterminés tous à la fois; le résidu des impies sera exerminé.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
Le salut des justes vient du Seigneur; il est leur appui au temps de l'affliction,
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
Et le Seigneur les soutiendra, et il les délivrera, et il les ravira aux pécheurs, et il les sauvera, parce qu'ils ont espéré en lui.