< Masalimo 37 >

1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
Of David. Do not fret over those who do evil; do not envy those who do wrong.
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
For they wither quickly like grass and wilt like tender plants.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Trust in the LORD and do good; dwell in the land and cultivate faithfulness.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
Delight yourself in the LORD, and He will give you the desires of your heart.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Commit your way to the LORD; trust in Him, and He will do it.
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
He will bring forth your righteousness like the dawn, your justice like the noonday sun.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Be still before the LORD and wait patiently for Him; do not fret when men prosper in their ways, when they carry out wicked schemes.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Refrain from anger and abandon wrath; do not fret—it can only bring harm.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
For the evildoers will be cut off, but those who hope in the LORD will inherit the land.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
Yet a little while, and the wicked will be no more; though you look for them, they will not be found.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
But the meek will inherit the land and delight in abundant prosperity.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
The wicked scheme against the righteous and gnash their teeth at them,
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
but the Lord laughs, seeing that their day is coming.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
The wicked have drawn the sword and bent the bow to bring down the poor and needy, to slay those whose ways are upright.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
But their swords will pierce their own hearts, and their bows will be broken.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Better is the little of the righteous than the abundance of many who are wicked.
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
For the arms of the wicked will be broken, but the LORD upholds the righteous.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
The LORD knows the days of the blameless, and their inheritance will last forever.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
In the time of evil they will not be ashamed, and in the days of famine they will be satisfied.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
But the wicked and enemies of the LORD will perish like the glory of the fields. They will vanish; like smoke they will fade away.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
The wicked borrow and do not repay, but the righteous are gracious and giving.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
Surely those He blesses will inherit the land, but the cursed will be destroyed.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
The steps of a man are ordered by the LORD who takes delight in his journey.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
Though he falls, he will not be overwhelmed, for the LORD is holding his hand.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
I once was young and now am old, yet never have I seen the righteous abandoned or their children begging for bread.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
They are ever generous and quick to lend, and their children are a blessing.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Turn away from evil and do good, so that you will abide forever.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
For the LORD loves justice and will not forsake His saints. They are preserved forever, but the offspring of the wicked will be cut off.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
The righteous will inherit the land and dwell in it forever.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
The mouth of the righteous man utters wisdom, and his tongue speaks justice.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
The law of his God is in his heart; his steps do not falter.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
Though the wicked lie in wait for the righteous, and seek to slay them,
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
the LORD will not leave them in their power or let them be condemned under judgment.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Wait for the LORD and keep His way, and He will raise you up to inherit the land. When the wicked are cut off, you will see it.
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
I have seen a wicked, ruthless man flourishing like a well-rooted native tree,
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
yet he passed away and was no more; though I searched, he could not be found.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Consider the blameless and observe the upright, for posterity awaits the man of peace.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
But the transgressors will all be destroyed; the future of the wicked will be cut off.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
The salvation of the righteous is from the LORD; He is their stronghold in time of trouble.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
The LORD helps and delivers them; He rescues and saves them from the wicked, because they take refuge in Him.

< Masalimo 37 >