< Masalimo 37 >

1 Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
[A Psalm] of David. Fret not thyself because of evil-doers, Neither be thou envious against them that work unrighteousness.
2 pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
For they shall soon be cut down like the grass, And wither as the green herb.
3 Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
Trust in Jehovah, and do good; Dwell in the land, and feed on [his] faithfulness.
4 Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
Delight thyself also in Jehovah; And he will give thee the desires of thy heart.
5 Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
Commit thy way unto Jehovah; Trust also in him, and he will bring it to pass.
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
And he will make thy righteousness to go forth as the light, And thy justice as the noonday.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
Rest in Jehovah, and wait patiently for him: Fret not thyself because of him who prospereth in his way, Because of the man who bringeth wicked devices to pass.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
Cease from anger, and forsake wrath: Fret not thyself, [it tendeth] only to evil-doing.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
For evil-doers shall be cut off; But those that wait for Jehovah, they shall inherit the land.
10 Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
For yet a little while, and the wicked shall not be: Yea, thou shalt diligently consider his place, and he shall not be.
11 Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
But the meek shall inherit the land, And shall delight themselves in the abundance of peace.
12 Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
The wicked plotteth against the just, And gnasheth upon him with his teeth.
13 koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
The Lord will laugh at him; For he seeth that his day is coming.
14 Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
The wicked have drawn out the sword, and have bent their bow, To cast down the poor and needy, To slay such as are upright in the way.
15 Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
Their sword shall enter into their own heart, And their bows shall be broken.
16 Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
Better is a little that the righteous hath Than the abundance of many wicked.
17 pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
For the arms of the wicked shall be broken; But Jehovah upholdeth the righteous.
18 Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
Jehovah knoweth the days of the perfect; And their inheritance shall be for ever.
19 Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
They shall not be put to shame in the time of evil; And in the days of famine they shall be satisfied.
20 Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
But the wicked shall perish, And the enemies of Jehovah shall be as the fat of lambs: They shall consume; in smoke shall they consume away.
21 Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
The wicked borroweth, and payeth not again; But the righteous dealeth graciously, and giveth.
22 Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
For such as are blessed of him shall inherit the land; And they that are cursed of him shall be cut off.
23 Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
A man’s goings are established of Jehovah; And he delighteth in his way.
24 ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
Though he fall, he shall not be utterly cast down; For Jehovah upholdeth him with his hand.
25 Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
I have been young, and now am old; Yet have I not seen the righteous forsaken, Nor his seed begging bread.
26 Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
All the day long he dealeth graciously, and lendeth; And his seed is blessed.
27 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
Depart from evil, and do good; And dwell for evermore.
28 Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
For Jehovah loveth justice, And forsaketh not his saints; They are preserved for ever: But the seed of the wicked shall be cut off.
29 olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
The righteous shall inherit the land, And dwell therein for ever.
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
The mouth of the righteous talketh of wisdom, And his tongue speaketh justice.
31 Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
The law of his God is in his heart; None of his steps shall slide.
32 Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
The wicked watcheth the righteous, And seeketh to slay him.
33 koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
Jehovah will not leave him in his hand, Nor condemn him when he is judged.
34 Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
Wait for Jehovah, and keep his way, And he will exalt thee to inherit the land: When the wicked are cut off, thou shalt see it.
35 Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
I have seen the wicked in great power, And spreading himself like a green tree in its native soil.
36 Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
But one passed by, and, lo, he was not: Yea, I sought him, but he could not be found.
37 Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
Mark the perfect man, and behold the upright; For there is a [happy] end to the man of peace.
38 Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
As for transgressors, they shall be destroyed together: The end of the wicked shall be cut off.
39 Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
But the salvation of the righteous is of Jehovah: He is their stronghold in the time of trouble.
40 Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.
And Jehovah helpeth them, and rescueth them: He rescueth them from the wicked, and saveth them, Because they have taken refuge in him.

< Masalimo 37 >